Salimo 122:1-9

  • Pemphero lopempherera mtendere wa Yerusalemu

    • Anasangalala pamene ankapita kunyumba ya Yehova (1)

    • Mzinda womangidwa ngati chinthu chimodzi chogwirizana (3)

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. Salimo la Davide. 122  Ndinasangalala pamene anandiuza kuti: “Tiyeni tipite kunyumba ya Yehova.”+  2  Ndipo tsopano mapazi athu aimaPamageti ako iwe Yerusalemu.+  3  Yerusalemu ndi mzinda umene wamangidwaNgati chinthu chimodzi chogwirizana.+  4  Mafuko apita kumeneko,Mafuko a Ya,*Mogwirizana ndi chilamulo chimene* Isiraeli anapatsidwaKuti azikatamanda dzina la Yehova.+  5  Chifukwa kumeneko nʼkumene kunaikidwa mipando yachiweruzo,+Mipando yachifumu ya nyumba ya Davide.+  6  Pemphererani mtendere wa Yerusalemu.+ Amene amakukonda, mzinda iwe, adzakhala otetezeka.  7  Mtendere upitirize kukhala mʼmalo ako otchingidwa ndi mpanda wolimba,Chitetezo chipitirize kukhala munsanja zako zokhala ndi mpanda wolimba.  8  Chifukwa choti ndimakonda abale anga komanso anzanga ndikunena kuti: “Mumzindawu mukhale mtendere.”  9  Chifukwa choti ndimakonda nyumba ya Yehova Mulungu wathu,+Ndidzapitiriza kukufunira zabwino.

Mawu a M'munsi

“Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.
Kapena kuti, “zikumbutso zimene.”