Salimo 60:1-12

  • Mulungu amagonjetsa adani

    • Chipulumutso chochokera kwa munthu nʼchopanda pake (11)

    • “Mulungu adzatipatsa mphamvu” (12)

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe motsatira kaimbidwe ka nyimbo ya “Duwa la Chikumbutso.” Mikitamu.* Salimo la Davide. Nyimbo yophunzitsira. Pa nthawi imene Davide anali pankhondo ndi Aramu-naharaimu ndi Aramu-Zoba, ndipo Yowabu anabwerera nʼkukapha Aedomu 12,000 mʼchigwa cha Mchere.+ 60  Inu Mulungu, munatikana ndipo munatigonjetsa.+ Munatikwiyira. Koma tsopano tiloleni tibwerere kwa inu.  2  Mwachititsa kuti dziko lapansi ligwedezeke ndipo mwalingʼamba. Tsekani mingʼalu yake, chifukwa likugwa.  3  Mwachititsa kuti anthu anu akumane ndi mavuto. Mwatimwetsa vinyo amene wachititsa kuti tiziyenda dzandidzandi.+  4  Perekani* chizindikiro kwa anthu amene amakuopaniKuti athawe ndi kuzemba uta. (Selah)  5  Kuti anthu amene mumawakonda apulumutsidwe,Tipulumutseni ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutiyankhe.+  6  Popeza ndi woyera,* Mulungu walankhula kuti: “Ndidzasangalala popereka Sekemu ngati cholowa,+Ndipo ndidzayezera anthu anga malo mʼchigwa cha Sukoti.+  7  Giliyadi ndi wanga, ngati mmene zilili ndi Manase,+Ndipo Efuraimu ndi chipewa choteteza* mutu wanga.Yuda akuimira mphamvu zanga zolamula.+  8  Mowabu ndi beseni langa losambiramo.+ Edomu ndidzamuponyera nsapato zanga.+ Ndidzafuula mosangalala chifukwa chogonjetsa Filisitiya.”+  9  Ndi ndani amene adzandibweretse kumzinda wozunguliridwa ndi adani?* Ndi ndani amene adzanditsogolere mpaka kukafika ku Edomu?+ 10  Kodi si inu Mulungu amene munatikana,Mulungu wathu, amene simukutsogoleranso magulu athu ankhondo?+ 11  Tithandizeni pamene tikukumana ndi mavuto,Chifukwa chipulumutso chochokera kwa munthu nʼchopanda pake.+ 12  Mulungu adzatipatsa mphamvu,+Ndipo adzapondaponda adani athu.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “Mwapatsa.”
Mabaibulo ena amati, “Mʼmalo ake opatulika.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “malo achitetezo oteteza.”
Mabaibulo ena amati, “wotetezedwa.”