Salimo 17:1-15

  • Pemphero lopempha chitetezo

    • “Mwafufuza mtima wanga” (3)

    • “Mumthunzi wa mapiko anu” (8)

Pemphero la Davide. 17  Imvani dandaulo langa lopempha kuti mundichitire chilungamo, inu Yehova.Mvetserani kulira kwanga kopempha thandizo.Imvani pemphero langa lopanda chinyengo.+  2  Mupereke chigamulo chachilungamo mʼmalo mwa ine.+Maso anu aone kuti ndine wolungama.  3  Mwafufuza mtima wanga, mwandifufuza ngakhale usiku,+Ndipo mwandiyenga.+Mudzapeza kuti ndinalibe zolinga zochita choipa chilichonse.Ndipo pakamwa panga sipanachimwe.  4  Kunena za ntchito za anthu,Mogwirizana ndi mawu apakamwa panu, ndapewa kuyenda mʼnjira za wachifwamba.+  5  Ndithandizeni kuti ndipitirize kuyenda mʼnjira zanu,Kuti mapazi anga asapunthwe.+  6  Ine ndikuitana inu, chifukwa mudzandiyankha,+ inu Mulungu. Tcherani khutu* kwa ine. Imvani mawu anga.+  7  Sonyezani modabwitsa chikondi chanu chokhulupirika,+Inu Mpulumutsi wa anthu amene amathawira kudzanja lanu lamanjaKuthawa anthu amene akupandukirani.  8  Nditetezeni ngati mwana wa diso lanu,+Ndibiseni mumthunzi wa mapiko anu.+  9  Nditetezeni kwa anthu oipa amene akundiukira,Kwa adani* ochokera kufumbi amene andizungulira.+ 10  Mitima yawo siimva chisoni,*Ndipo amalankhula modzikuza ndi pakamwa pawo. 11  Tsopano adaniwo atizungulira,+Akufufuza mpata kuti atigwetse.* 12  Ali ngati mkango umene ukufunitsitsa kukhadzula nyama,Ngati mkango wamphamvu umene wabisalira nyama. 13  Nyamukani, inu Yehova, mulimbane naye+ nʼkumugwetsa.Ndipulumutseni kwa woipayo ndi lupanga lanu. 14  Ndipulumutseni ndi dzanja lanu, inu Yehova,Kwa anthu amʼdzikoli* amene gawo lawo lili mʼmoyo uno,+Anthu amene mwawakhutitsa ndi zinthu zabwino zimene mumapereka+Omwe amasiyira cholowa ana awo aamuna ochuluka. 15  Koma ine ndidzaona nkhope yanu mʼchilungamo.Ndikadzuka ndimadziwa kuti muli nane* ndipo ndimakhutira.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Weramani ndi kumvetsera.”
Kapena kuti, “adani amene akufuna moyo wanga.”
Kapena kuti, “Adzikuta ndi mafuta awo omwe.”
Kapena kuti, “atiponyere pansi.”
Kapena kuti, “amʼnthawi ino.”
Kapena kuti, “Ndikadzuka ndimakuonani.”