Salimo 139:1-24

Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide. 139  Inu Yehova, mwandifufuza ndipo mukundidziwa.+   Inu mumadziwa ndikakhala pansi kapena ndikaimirira.+Mumadziwa maganizo anga muli kutali.+   Mumandidziwa bwino pamene ndikuyenda komanso pamene ndikugona,+Ndipo njira zanga zonse mukuzidziwa bwino.+   Ndisananene kanthu,+Inu Yehova mumakhala mutadziwa kale zonse.+   Mwandizungulira,Ndipo mwaika dzanja lanu pa ine.   Kwa ine ndi zovuta kwambiri kuti ndidziwe zinthu zonsezi.+Ndi zapamwamba kwambiri moti sindingathe kuzifikira.+   Ndingapite kuti kuthawa mzimu wanu,+Ndipo ndingapite kuti kuthawa nkhope yanu?+   Ngati ndingakwere kumwamba, inu mudzakhala komweko.+Ndipo ngati ndingayale bedi langa ku Manda, taonani! inunso mudzakhala komweko.+   Ngati ndingakwere pamapiko+ a m’bandakucha,Kuti ndikakhale m’nyanja ya kutali kwambiri,+ 10  Kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,+Dzanja lanu lamanja lidzandigwira.+ 11  Ngati ndinganene kuti: “Ndithudi mdima undipeze mofulumira!”+Pamenepo mdima udzasanduka kuwala pa ine.+ 12  Ndipo mdimawo sudzakhala mdima wandiweyani kwa inu,+Koma usiku udzakuwalirani ngati masana.+Mdima udzangokhala ngati kuwala.+ 13  Inu munapanga impso zanga,+Ndipo munali kunditchinga m’mimba mwa mayi anga.+ 14  Ndidzakutamandani chifukwa munandipanga modabwitsa ndipo zimenezi zimandichititsa mantha.+Ntchito zanu ndi zodabwitsa,+Ndipo ine ndimadziwa bwino zimenezi.+ 15  Mafupa anga sanali obisika kwa inu+Pamene munali kundipanga m’malo obisika,+Pamene munali kundiwomba ngati nsalu m’malo apansi kwambiri+ padziko lapansi. 16  Maso anu anandiona pamene ndinali mluza,+Ndipo ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku lanu.M’bukumo munalembamo za masiku amene zinapangidwa+Koma panalibe ngakhale chiwalo chimodzi chimene chinali chitapangidwa. 17  Choncho kwa ine maganizo anu ndi ofunika kwambiri,+ inu Mulungu,Ndipo ndi ochuluka zedi.+ 18  Nditati ndiyese kuwawerenga, angakhale ochuluka kwambiri kuposa mchenga.+Podzuka ndingakhale ndikuwawerengabe.+ 19  Inu Mulungu, zikanakhala bwino mukanapha woipa.+Pamenepo anthu amene ali ndi mlandu wa magazi+ akanandichokera, 20  Anthu amene amanena zam’mutu mwawo zotsutsana ndi inu.+Adani anuwo+ agwiritsa ntchito dzina lanu mosasamala.+ 21  Inu Yehova, pajatu ine ndimadana ndi anthu amene amadana nanu kwambiri,+Ndipo anthu okupandukirani ndimanyansidwa nawo.+ 22  Ndimadana nawo kwambiri.+Kwa ine akhala adani enieni.+ 23  Ndifufuzeni, inu Mulungu, ndi kudziwa mtima wanga.+Ndisanthuleni ndi kudziwa malingaliro anga amene akundisowetsa mtendere,+ 24  Ndipo muone ngati mwa ine muli chilichonse chimene chikundichititsa kuyenda m’njira yoipa,+Ndipo munditsogolere m’njira+ yamuyaya.

Mawu a M'munsi