Salimo 58:1-11

Kwa wotsogolera nyimbo. “Musandiwononge.” Salimo la Davide. Mikitamu.* 58  Kodi mungalankhule bwanji za chilungamo mutakhala chete?+Kodi mungaweruze molungama, inu ana a anthu?+   Ayi! Inu mukuchita zosalungama padziko lapansi mogwirizana ndi zimene mtima wanu ukufuna,+Ndipo mukukonza njira zochitira chiwawa ndi manja anu.+   Oipa akhala opotoka maganizo kuyambira ali m’mimba.+Iwo asochera kuyambira ali m’mimba,Ndipo amalankhula zabodza.+   Iwo ali ndi poizoni ngati wa njoka,+Ndipo ndi ogontha ngati njoka ya mamba imene yatseka makutu ake,+   Imene singamve mawu a munthu wamatsenga,+Ngakhale wina wanzeru ataimanga ndi mphamvu zamatsenga.+   Inu Mulungu, agululeni mano m’kamwa mwawo.+Inu Yehova, thyolani nsagwada za mkango wamphamvu.   Asungunuke ndi kupita ngati madzi.+Mulungu akunge uta woponyera mivi yake pamene adaniwo akugwa.+   Woipayo amayenda ngati nkhono imene ikusungunuka.Iwo sadzaona dzuwa ngati mwana wa mayi amene wapita padera.+   Miphika yanu isanayambe kumva kutentha kwa moto wa mitengo yaminga,+Mulungu adzauluza ndi mphepo yamkuntho mitengo yaiwisi yaminga pamodzi ndi imene ikuyaka.+ 10  Wolungama adzasangalala chifukwa chakuti waona oipa akupatsidwa chilango.+Adzasambitsa mapazi ake m’magazi a anthu oipa.+ 11  Ndipo mtundu wa anthu udzati:+ “Ndithudi wolungama adzalandira mphoto.+Ndithudi pali Mulungu amene akuweruza dziko lapansi.”+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.