Salimo 130:1-8

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 130  Inu Yehova, pa nthawi imene zinthu zinandivuta kwambiri ndinaitana pa inu.+   Imvani mawu anga Yehova.+Makutu anu amve mawu anga ochonderera.+   Inu Ya, mukanakhala kuti mumayang’anitsitsa zolakwa,+Ndani akanaima pamaso panu, inu Yehova?+   Inu mumakhululukiradi,+Kuti anthu akuopeni.+   Ndayembekezera thandizo lanu, inu Yehova. Moyo wanga wayembekezera thandizo lanu.+Ine ndayembekezera mawu anu.+   Ndayembekezera Yehova+Kuposa alonda amene akuyembekezera kuti kuche,+Ndithu kuposa alonda amene akuyembekezera kuti kuche.+   Isiraeli ayembekezere Yehova,+Pakuti Yehova amasonyeza kukoma mtima kosatha.+Iye ali ndi mphamvu zochuluka zowombolera anthu ake.+   Iye adzawombola Isiraeli ku zolakwa zake zonse.+

Mawu a M'munsi