Salimo 123:1-4

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 123  Ndakweza maso anga kuyang’ana inu,+Kuyang’ana inu amene mukukhala kumwamba.+   Taonani! Monga mmene maso a atumiki amayang’anira dzanja la mbuye wawo,+Mmene maso a kapolo wamkazi amayang’anira dzanja la mbuye wake wamkazi,+Momwemonso, maso athu adzayang’ana kwa Yehova Mulungu wathu,+Kufikira atatikomera mtima.+   Tikomereni mtima, inu Yehova, tikomereni mtima,+Pakuti tanyozeka kwambiri.+   Moyo wathu wasautsika kwambiri chifukwa cha kunyoza kwa anthu amene akukhala mosatekeseka,+Ndiponso chifukwa cha kunyoza kwa anthu odzikuza.+

Mawu a M'munsi