Salimo 128:1-6

Nyimbo Yokwerera Kumzinda. 128  Wodala ndi aliyense woopa Yehova,+Amene amayenda m’njira za Mulungu.+   Pakuti udzadya zipatso za ntchito ya manja ako.+Udzakhala wodala ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.+   Mkazi wako adzakhala ngati mtengo wa mpesa wobala zipatso+Mkati mwa nyumba yako.Ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya maolivi+ kuzungulira tebulo lako.   Taonani! Mwamuna aliyense wamphamvu woopa Yehova+Adzadalitsidwa mwa njira imeneyi.+   Yehova adzakudalitsa ali ku Ziyoni.+Komanso usangalale ndi zinthu zabwino za mu Yerusalemu masiku onse a moyo wako,+   Ndipo uone ana a ana ako.+Mtendere ukhale pa Isiraeli.+

Mawu a M'munsi