Salimo 98:1-9

Nyimbo. 98  IMBIRANI Yehova nyimbo yatsopano,+Pakuti zimene wachita ndi zodabwitsa.+Dzanja lake lamanja, ndithu mkono wake woyera, wabweretsa chipulumutso.+   Yehova wachititsa chipulumutso chake kudziwika.+Chilungamo chake wachisonyeza ku mitundu ya anthu.+   Iye wakumbukira lonjezo lake losonyeza kukoma mtima kosatha ndi kukhulupirika kwake ku nyumba ya Isiraeli.+Malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.+   Fuulirani Yehova mosangalala chifukwa wapambana, inu nonse anthu a padziko lapansi.+Kondwerani, fuulani mosangalala ndi kuimba nyimbo zomutamanda.+   Imbirani Yehova nyimbo zomutamanda ndi zeze,+Muimbireni nyimbo ndi zeze ndi kumutamanda ndi nyimbo zokoma.+   Fuulani mwa kuimba malipenga ndi mphalasa.*+Fuulani mosangalala pamaso pa Mfumu Yehova, chifukwa wapambana.   Nyanja ndi zonse zili mmenemo zichite mkokomo,+Chimodzimodzinso mtunda ndi zonse zokhala kumeneko.+   Mitsinje iwombe m’manja,Mapiri onse afuule pamodzi mokondwera pamaso pa Yehova.+   Pakuti iye wabwera kudzaweruza dziko lapansi.+Adzaweruza dziko mwachilungamo,+Ndipo adzaweruza mitundu ya anthu molungama.+

Mawu a M'munsi

“Mphalasa” ndi lipenga lopangidwa ndi nyanga ya nkhosa.