Yeremiya 21:1-14
21 Yeremiya analandira mawu ochokera kwa Yehova pamene Mfumu Zedekiya+ inatumiza Pasuri+ mwana wa Malikiya ndi Zefaniya+ mwana wa Maaseya, wansembe, kuti akamupemphe kuti:
2 “Chonde tifunsire kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara,* mfumu ya ku Babulo, akufuna kuchita nafe nkhondo.+ Mwina Yehova atichitira imodzi mwa ntchito zake zodabwitsa moti Nebukadinezarayo atichokera.”+
3 Yeremiya anawauza kuti: “Mukauze Zedekiya kuti,
4 ‘Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Ine ndichititsa zida zankhondo zimene zili mʼmanja mwanu kukutembenukirani. Zimenezi ndi zida zimene mukugwiritsa ntchito pomenyana ndi mfumu ya Babulo+ ndi Akasidi amene akuzungulirani kunja kwa mpanda wanu. Ndipo ine ndidzasonkhanitsa zidazo pakati pa mzindawu.
5 Ine ndidzamenyana nanu+ ndi mkono wotambasula ndiponso dzanja lamphamvu. Ndidzachita zimenezi nditakwiya, nditapsa mtima komanso ndili ndi ukali waukulu.+
6 Ndidzapha onse okhala mumzindawu, anthu komanso nyama. Adzafa ndi mliri waukulu.”’*+
7 ‘Yehova wanena kuti: “Kenako Zedekiya mfumu ya Yuda, atumiki ake ndi anthu amumzindawu, onse amene adzapulumuke ku mliri, lupanga ndi njala yaikulu, ndidzawapereka mʼmanja mwa Mfumu Nebukadinezara* ya ku Babulo. Ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo komanso mʼmanja mwa amene akufuna kuchotsa moyo wawo.+ Nebukadinezara adzawapha ndi lupanga ndipo sadzawamvera chisoni, kuwakomera mtima kapena kuwachitira chifundo.”’+
8 Ndipo anthu awa uwauze kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Ine ndikuika njira ya moyo ndi njira ya imfa pamaso panu.
9 Anthu amene adzatsale mumzindawu adzafa ndi lupanga, njala ndiponso mliri. Koma aliyense amene adzatuluke nʼkupita kukadzipereka mʼmanja mwa Akasidi amene akuzungulirani, adzakhalabe ndi moyo. Iye adzapulumutsa moyo wake.”’+
10 ‘“Ndatsimikiza kubweretsa tsoka pamzinda uwu, osati zinthu zabwino,”*+ akutero Yehova. “Mzindawu udzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya Babulo+ ndipo adzauwotcha ndi moto.”+
11 A mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ukawauze kuti: Imvani zimene Yehova wanena.
12 Inu a mʼnyumba ya Davide, Yehova wanena kuti:
“Mʼmawa uliwonse muziweruza mwachilungamoNdipo muzipulumutsa munthu amene akuberedwa mʼmanja mwa anthu akuba mwachinyengo,+Kuti mkwiyo wanga usayake ngati moto.+Usayake popanda aliyense wouzimitsaChifukwa cha zinthu zoipa zimene mukuchita.”’+
13 ‘Iwe amene umakhala mʼchigwa, ine ndakuukira,Iwe thanthwe limene lili pamalo afulati,’ akutero Yehova.
‘Koma inu amene mukunena kuti: “Kodi ndi ndani amene adzabwere kuno kuti atiukire?
Ndipo ndi ndani amene adzabwere mʼmalo athu okhala?”
14 Ndidzakupatsani chilangoMogwirizana ndi zochita zanu,’+ akutero Yehova.
‘Ndipo ndidzayatsa moto munkhalango za mzindawu,Moti udzapsereza zinthu zonse zimene zili pafupi ndi mzindawu.’”+
Mawu a M'munsi
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
^ Kapena kuti, “matenda aakulu.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Nkhope yanga ili pa mzinda uwu kuti ndiuwononge.”