Yeremiya 14:1-22

  • Chilala, njala ndi lupanga (1-12)

  • Aneneri abodza adzawonongedwa (13-18)

  • Yeremiya anavomereza kuti anthuwo anali ochimwa (19-22)

14  Mawu amene Yehova anauza Yeremiya pa nkhani ya chilala ndi awa:+  2  Yuda akulira maliro+ ndipo mageti ake agwa. Agwa pansi nʼkumalira momvetsa chisoni,Ndipo anthu a ku Yerusalemu akulira.  3  Anthu awo olemekezeka amatuma antchito awo kuti akatunge madzi. Antchitowo amapita kuzitsime koma sapezako madzi. Amabwerako ndi ziwiya zopanda kanthu. Iwo achita manyazi ndipo akhumudwa,Moti aphimba mitu yawo.  4  Alimi ataya mtima ndipo aphimba mitu yawoChifukwa chakuti mʼdzikomo simunagwe mvula+Ndipo nthaka yangʼambikangʼambika.  5  Ngakhale mbawala yaikazi yasiya mwana wake wobadwa kumene mʼthengoChifukwa kulibe msipu.  6  Abulu amʼtchire angoima mʼmapiri opanda kanthu. Akupuma mwawefuwefu ngati mimbulu.Maso awo achita mdima chifukwa kulibe msipu.+  7  Ngakhale kuti machimo athu akuchitira umboni kuti ndife olakwa,Inu Yehova, chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.+ Chifukwa zochita zathu zosonyeza kusakhulupirika nʼzambiri,+Ndipo takuchimwirani.  8  Inu chiyembekezo cha Isiraeli, Mpulumutsi wake+ pa nthawi yamavuto,Nʼchifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdzikoli?Nʼchifukwa chiyani mukukhala ngati munthu wapaulendo amene waima kuti agone usiku umodzi wokha?  9  Nʼchifukwa chiyani mukukhala ngati munthu wothedwa nzeru,Ndiponso ngati munthu wamphamvu amene sangathe kupulumutsa anthu ake? Komatu inu Yehova muli pakati pathu,+Ndipo ife timadziwika ndi dzina lanu.+ Musatisiye. 10  Ponena za anthu awa Yehova wanena kuti: “Iwo amakonda kumangoyendayenda+ ndipo samatha kudziletsa kuti asamayendeyende.+ Choncho Yehova sakusangalala nawo.+ Tsopano iye akumbukira zolakwa zawo ndipo awalanga chifukwa cha machimo awo.”+ 11  Kenako Yehova anandiuza kuti: “Usapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.+ 12  Akamasala kudya, ine sindimvetsera kuchonderera kwawo.+ Akamapereka nsembe zopsereza zathunthu ndi nsembe zambewu, ine sindisangalala nazo+ ndipo ndiwawononga ndi lupanga, njala yaikulu ndiponso mliri.”*+ 13  Nditamva zimenezi ndinanena kuti: “Mayo ine! Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa. Aneneri akuuza anthuwo kuti, ‘Simudzawonongedwa ndi lupanga ndipo njala yaikulu sidzakugwerani, koma Mulungu adzakupatsani mtendere weniweni mʼmalo ano.’”+ 14  Ndiyeno Yehova anandiyankha kuti: “Aneneriwo akulosera zinthu zabodza mʼdzina langa.+ Ine sindinawatume, kuwalamula kapena kulankhula nawo.+ Maulosi amene akukuuzaniwo ndi masomphenya abodza, maulosi opanda pake ndi chinyengo chamumtima mwawo.+ 15  Choncho Yehova wanena kuti: ‘Ponena za aneneri amene akulosera mʼdzina langa ngakhale kuti sindinawatume, amenenso akunena kuti lupanga kapena njala sizidzafika mʼdziko lino, ine ndikuti aneneri amenewo adzaphedwa ndi lupanga ndiponso njala yaikulu.+ 16  Anthu amene akuwauza maulosi awowo, adzafa ndi njala komanso lupanga ndipo mitembo yawo idzatayidwa mʼmisewu ya Yerusalemu. Sipadzakhala wowaika mʼmanda,+ iwowo, akazi awo, ana awo aamuna kapena ana awo aakazi chifukwa ndidzawatsanulira tsoka limene akuyenera kulandira.’+ 17  Anthu awa uwauze kuti,‘Maso anga atulutse misozi usiku ndi masana ndipo asasiye,+Chifukwa mwana wamkazi wa anthu anga, yemwe ndi namwali, waphwanyidwa kotheratu+Ndipo ali ndi bala lalikulu kwambiri. 18  Ndikapita kunja kwa mzinda,Ndikuona anthu ophedwa ndi lupanga.+ Ndipo ndikalowa mumzinda,+Ndikuona matenda obwera chifukwa cha njala. Aneneri komanso ansembe, onse apita kudziko lachilendo limene sakulidziwa.’”+ 19  Kodi Yuda mwamukaniratu, kapena kodi mukunyansidwa ndi Ziyoni?+ Nʼchifukwa chiyani mwatilanga chonchi moti sitingathenso kuchira?+ Timayembekezera mtendere, koma palibe chabwino chilichonse chimene chachitika.Timayembekezera kuchiritsidwa, koma tikungoona zinthu zochititsa mantha.+ 20  Inu Yehova, ife tikuvomereza zinthu zoipa zimene tachitaKomanso kulakwa kwa makolo athu,Chifukwa takuchimwirani.+ 21  Koma chifukwa cha dzina lanu, musatikane.+Musachititse manyazi mpando wanu wachifumu waulemerero. Kumbukirani pangano limene munachita ndi ife ndipo musaliphwanye.+ 22  Kodi pa mafano opanda pake a mitundu ya anthu pali fano lililonse limene lingagwetse mvula?Kapena kodi kumwamba pakokha kungagwetse mvula yamvumbi? Kodi si inu nokha, Yehova Mulungu wathu, amene mumachititsa zimenezi?+ Chiyembekezo chathu chili mwa inuChifukwa inu nokha ndi amene mumachita zonsezi.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “matenda.”