Genesis 23:1-20

23  Sara anakhala ndi moyo zaka 127. Zimenezi ndizo zinali zaka za moyo wake.+  Sara anamwalirira ku Kiriyati-ariba,+ kapena kuti ku Heburoni,+ m’dziko la Kanani.+ Pamenepo Abulahamu analowa muhema kukamulira Sara.  Ndiyeno Abulahamu anachoka pamene panali mtembo wa mkazi wake n’kupita kukalankhula ndi ana a Heti,+ kuti:  “Ine ndinadzakhala kwanu kuno ngati mlendo.+ Choncho ndigawireniko malo kuti ndikhale ndi manda angaanga, ndiikemo mkazi wanga.”*+  Ana a Heti anayankha Abulahamu kuti:  “Timvereni mbuyathu.+ Inu ndinu mtsogoleri woikidwa ndi Mulungu.+ Sankhani manda abwino koposa pa manda amene tili nawo kuti muikemo malemuwo.+ Palibe aliyense wa ife amene angakanize manda ake kuti muikemo malemuwo.”+  Pamenepo Abulahamu anaimirira n’kugwada pansi pamaso pa eni dzikowo,+ ana a Heti.+  Iye analankhula nawo kuti: “Ngati mukuvomera kuti ndiike m’manda malemu mkazi wanga, ndimvereni ndipo mundipemphere kwa Efuroni mwana wa Zohari.+  Mundipemphere kuti andigulitse phanga lake la Makipela+ limene lili m’malire a malo ake. Andigulitse pa mtengo wake wonse inu mukuona, kuti ndiikemo malemu mkazi wanga.”+ 10  Pa nthawiyi n’kuti Efuroni atakhala pansi pakati pa ana a Heti. Choncho Efuroni Mhiti+ anayankha Abulahamu, ana a Hetiwo akumva limodzi ndi onse amene analowa pachipata cha mzinda wake.+ Iye anati: 11  “Ayi mbuyanga! Ndimvereni. Malowo, pamodzi ndi phanga limene lili pamalopo, ndikupatsani pamaso pa anthu a mtundu wangawa.+ Kaikeni malemuwo.” 12  Pamenepo Abulahamu anagwada pamaso pa eni dzikowo. 13  Kenako iye analankhula kwa Efuroni pamaso pa eni dzikowo kuti: “Ndimvere chonde. Ine ndigulabe malowo. Landira silivayu+ kuti ndikaike mkazi wanga kumeneko.” 14  Ndiyeno Efuroni anayankha Abulahamu kuti: 15  “Ndimvereni mbuyanga. Malowo mtengo wake ndi siliva wolemera masekeli* 400. Koma zimenezo sindiyo nkhani yaikulu pakati pa ine ndi inu. Kaikeni malemuwo.”+ 16  Chotero Abulahamu anamveradi Efuroni, n’kumuyezera siliva wokwanira mtengo umene Efuroniyo ananena pamaso pa ana a Heti. Anamuyezera siliva wolemera masekeli 400, malinga ndi muyezo wovomerezeka ndi amalonda pa nthawiyo.+ 17  Chotero malo a Efuroni amene anali ku Makipela moyang’anizana ndi Mamure, ndiponso phanga limene linali mmenemo, komanso mitengo yonse imene inali mkati mwa malire onse a malowo,+ anatsimikizirika+ 18  pamaso pa ana a Heti ndi onse amene analowa pachipata cha mzinda, kuti Abulahamu ndiye wagula malowo ndipo ndi ake.+ 19  Zitatero, Abulahamu anaika Sara mkazi wake m’manda kuphanga la Makipela, moyang’anizana ndi Mamure, kapena kuti Heburoni, m’dziko la Kanani.+ 20  Chotero ana a Heti anagulitsa kwa Abulahamu malowo ndi phanga limene linali pamenepo, ndipo mkazi wake anamuika m’manda kumeneko.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “ndiike malemu anga kuti ndisawaonenso.”
“Sekeli” unali muyezo wachiheberi wa kulemera kwa chinthu ndi wotchulira ndalama. Sekeli imodzi inali yofanana ndi magalamu 11.4, ndipo mtengo wake unali wofanana ndi madola 2.20 a ku America.