Genesis 10:1-32

10  Tsopano nayi mbiri ya ana a Nowa,+ omwe ndi Semu, Hamu ndi Yafeti. Pambuyo pa chigumula, iwowa anayamba kubereka ana.+  Ana a Yafeti anali Gomeri,+ Magogi,+ Madai,+ Yavani,+ Tubala,+ Meseke+ ndi Tirasi.+  Ana a Gomeri anali Asikenazi,+ Rifati+ ndi Togarima.+  Ana a Yavani anali Elisaha,+ Tarisi,+ Kitimu+ ndi Dodanimu.+  Kuchokera mwa amenewa, anthu anafalikira m’zilumba* m’madera awo malinga ndi zilankhulo zawo, mabanja awo ndi mitundu yawo.  Ana a Hamu anali Kusi,+ Miziraimu,+ Puti+ ndi Kanani.+  Ana a Kusi anali Seba,+ Havila, Sabita, Raama+ ndi Sabiteka. Ana a Raama anali Sheba ndi Dedani.+  Kusi anabereka Nimurodi,+ amene anali woyamba kukhala wamphamvu padziko lapansi.  Iye anakhala mlenje wamphamvu wotsutsana ndi Yehova. N’chifukwa chake pali mawu akuti: “Monga Nimurodi mlenje wamphamvu wotsutsana ndi Yehova.”+ 10  Ufumu wake unayambira ku Babele,+ Ereke,+ Akadi mpaka ku Kaline m’dziko la Sinara.+ 11  Kuchokera m’dzikoli analowera ku Asuri+ kumene anamanga Nineve,+ Rehoboti-iri, Kala, 12  komanso Resene wa pakati pa Nineve ndi Kala. Umenewu unali mzinda waukulu. 13  Miziraimu+ anabereka Ludimu,+ Anamimu, Lehabimu, Nafituhimu,+ 14  Patirusimu+ ndi Kasiluhimu+ (Afilisiti+ anachokera mwa iyeyu), ndiponso Kafitorimu.+ 15  Kanani anabereka Sidoni+ mwana wake woyamba, kenako anabereka Heti.+ 16  Anaberekanso Ayebusi,+ Aamori,+ Agirigasi, 17  Ahivi,+ Aariki, Asini, 18  Aarivadi,+ Azemari ndi Ahamati,+ ndipo pambuyo pake, mabanja a Akanani anabalalikana. 19  Choncho malire a dziko la Akanani anachokera ku Sidoni mpaka ku Gerari+ kufupi ndi Gaza,+ n’kukafika ku Sodomu ndi Gomora+ mpakanso ku Adima+ ndi Zeboyimu,+ kufupi ndi Lasa. 20  Amenewa ndiwo anali ana a Hamu monga mwa mabanja awo, monga mwa zilankhulo zawo, m’mayiko awo, mwa mitundu yawo. 21  Nayenso Semu, kholo la ana onse a Ebere,+ anali ndi mbadwa zake. Semu anali mng’ono wake wa Yafeti, amene anali wamkulu pa onse. 22  Ana a Semu anali Elamu,+ Ashuri,+ Aripakisadi,+ Ludi ndi Aramu. 23  Ana a Aramu anali Uzi, Huli, Geteri ndi Masi.+ 24  Aripakisadi anabereka Shela+ ndipo Shela anabereka Ebere. 25  Ebere anabereka ana awiri. Wina dzina lake anali Pelegi,*+ chifukwa m’masiku ake, dziko lapansi linagawikana.+ M’bale wakeyo dzina lake anali Yokitani.+ 26  Yokitani anabereka Alamodadi, Selefi, Hazaramaveti, Yera,+ 27  Hadoramu, Uzali, Dikila,+ 28  Obali, Abimaele, Sheba,+ 29  Ofiri,+ Havila+ ndi Yobabi.+ Onsewa anali ana a Yokitani. 30  Dziko lawo limene anali kukhala linayambira ku Mesa mpaka ku Sefara, dera lamapiri la Kum’mawa. 31  Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mabanja awo, zilankhulo zawo, m’mayiko awo, monga mwa mitundu yawo.+ 32  Amenewa ndiwo mabanja a ana a Nowa monga mwa mibadwo yawo, monganso mwa mitundu yawo. Ndipo kuchokera mwa iwowa, mitundu inafalikira padziko lapansi pambuyo pa chigumula.+

Mawu a M'munsi

Mawu omasuliridwa kuti “zilumba” pano kwenikweni amatanthauza madera a m’mphepete mwa nyanja.
Dzina lakuti “Pelegi” limatanthauza “Kugawika” ndiponso “Mfuleni.”