Genesis 33:1-20
33 Tsopano Yakobo anakweza maso ake n’kuona Esau akubwera limodzi ndi amuna 400.+ Ataona choncho, anagawa ana ake n’kuwapereka kwa Leya, kwa Rakele, ndi kwa akapolo ake awiri aja.+
2 Akapolowo ndi ana awo anawaika patsogolo penipeni,+ Leya ndi ana ake anawaika pakati,+ ndipo Rakele ndi Yosefe anawaika pambuyo.+
3 Koma iyeyo anapita patsogolo pawo, n’kuyamba kugwada, n’kumaweramitsa nkhope yake pansi mpaka nthawi 7. Anachita zimenezi mpaka kufika pafupi ndi m’bale wakeyo.+
4 Esau anathamanga kudzakumana naye,+ ndipo anamukumbatira+ ndi kum’psompsona. Atakumbatirana, onse awiri anagwetsa misozi kwambiri.
5 Kenako, Esau anakweza maso ake n’kuona akazi ndi ana. Ndiyeno anafunsa Yakobo kuti: “Nanga amene uli nawowa ndani?” Iye anayankha kuti: “Amenewa ndi ana amene Mulungu wapatsa ine kapolo wanu.”+
6 Pamenepo akapolo aja anafika pafupi limodzi ndi ana awo n’kugwada pansi.
7 Nayenso Leya anafika pafupi limodzi ndi ana ake n’kugwada pansi. Potsirizira pake, Yosefe ndi Rakele anafika pafupi, nawonso n’kugwada pansi.+
8 Tsopano Esau anafunsa kuti: “Nanga n’chifukwa chiyani watumiza khamu lonse limene ndakumana nalo lija?”+ Poyankha iye anati: “Ndachita zimenezi kuti mundikomere mtima mbuyanga.”+
9 Ndiyeno Esau anati: “Ziweto ndili nazo zambiri, m’bale wanga.+ Zako ndi zako, ukhale nazo.”
10 Koma Yakobo anati: “Ayi chonde, musatero. Ngati mwandikomeradi mtima,+ landirani mphatso yangayi, popeza cholinga chake chinali chakuti ndione nkhope yanu, ndipo ndaionadi. Zili ngati ndaona nkhope ya Mulungu, chifukwa mwandilandira ndi manja awiri.+
11 Chonde, landirani mphatso yokufunirani mafuno abwinoyi kuchokera kwa ine,+ chifukwa Mulungu wandikomera mtima, ndipo wandipatsa chilichonse.”+ Anamuumirizabe mpaka analandira mphatsoyo.+
12 Pambuyo pake Esau anati: “Tiye tinyamuke tizipita, ine nditsogole.”
13 Koma Yakobo anati: “Monga mukudziwa mbuyanga, anawa ndi osakhwima, komanso ndili ndi nkhosa ndi ng’ombe zoyamwitsa.+ Tikaziyendetsa mofulumira kwambiri, ngakhale tsiku limodzi lokha, ndithu zifa zonse.+
14 Chonde mbuyanga, tsogolani. Ine kapolo wanu ndizibwera m’mbuyo mwanu. Ndiziyenda pang’onopang’ono mogwirizana ndi mayendedwe a ziwetozi+ ndi kuyenda kwa anawa.+ Ndikakupezani ku Seiri, mbuyanga.”+
15 Ndiyeno Esau anati: “Chabwino, ndiye ndikupatseko ena mwa anyamata angawa kuti akuthandize.” Koma iye anati: “Ayi musachite kutero. Musavutike mbuyanga,+ ndiyenda bwinobwino.”
16 Choncho, Esau anatembenuka kubwerera ku Seiri tsiku lomwelo.
17 Tsopano Yakobo ananyamuka ulendo wopita ku Sukoti.+ Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake.+ N’chifukwa chake malowo anawatcha kuti Sukoti.*
18 Patapita nthawi, Yakobo anafika bwinobwino kumzinda wa Sekemu,+ m’dziko la Kanani,+ akuchokera ku Padana-ramu.+ Atafika, anamanga msasa pafupi ndi mzindawo.
19 Kenako anagula malo ndipo anamangapo msasa. Anawagula ndi ndalama zasiliva 100, kwa ana a Hamori, bambo wake wa Sekemu.+
20 Atatero, anamangapo guwa lansembe n’kulitcha Mulungu, Mulungu wa Isiraeli.+
Mawu a M'munsi
^ Dzina lakuti “Sukoti” limatanthauza “Makola” ndiponso “Makola Adenga.”