Genesis 11:1-32

11  Tsopano dziko lonse lapansi linali ndi chilankhulo chimodzi ndipo anthu anali kugwiritsa ntchito mawu ofanana.  Pamene anthuwo analowera chakum’mawa, anapeza chigwa m’dera la Sinara+ n’kukhazikika kumeneko.  Kenako anauzana kuti: “Tiyeni tiumbe njerwa tiziotche.” Atatero, anayamba kumanga ndi njerwa, n’kumagwiritsa ntchito phula ngati matope omangira.+  Ndiyeno anati: “Tiyeni timange mzinda wathuwathu, ndipo nsanja yake ikafike m’mwamba mwenimweni.+ Tikatero tidzipangira dzina loti titchuke nalo,+ ndipo sitibalalikana padziko lonse lapansi.”+  Kenako, Yehova anatsikirako kukaona mzinda ndi nsanja imene ana a anthu anali kumanga.+  Pamenepo Yehova anati: “Taonani! Izi n’zimene anthuwa ayamba kuchita popeza ndi amodzi ndipo onse ali ndi chilankhulo chimodzi.+ Mmene zililimu, angathe kuchita chilichonse chimene akuganiza.+  Choncho, tiyeni+ tipiteko kuti tikasokoneze+ chilankhulo chawo, kuti asamamvane polankhula.”+  Motero, Yehova anawabalalitsa pamalopo, kuti afalikire padziko lonse lapansi.+ Zitatero, iwo anasiya pang’onopang’ono kumanga mzindawo.+  Mzindawo unatchedwa Babele,+ chifukwa kumeneko, Yehova anasokoneza chilankhulo cha anthu onse, ndipo Yehova anabalalitsira+ anthuwo padziko lonse lapansi. 10  Tsopano iyi ndi mbiri ya Semu.+ Semu anali ndi zaka 100 pamene anabereka Aripakisadi,+ patapita zaka ziwiri pambuyo pa chigumula. 11  Atabereka Aripakisadi, Semu anakhalabe ndi moyo zaka zina 500. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi.+ 12  Aripakisadi atakhala ndi moyo zaka 35, anabereka Shela.+ 13  Atabereka Shela, Aripakisadi anakhalabe ndi moyo zaka zina 403. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 14  Shela atakhala ndi moyo zaka 30, anabereka Ebere.+ 15  Atabereka Ebere, Shela anakhalabe ndi moyo zaka zina 403. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 16  Ebere atakhala ndi moyo zaka 34, anabereka Pelegi.+ 17  Atabereka Pelegi, Ebere anakhalabe ndi moyo zaka zina 430. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 18  Pelegi atakhala ndi moyo zaka 30, anabereka Reu.+ 19  Atabereka Reu, Pelegi anakhalabe ndi moyo zaka zina 209. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 20  Reu atakhala ndi moyo zaka 32, anabereka Serugi.+ 21  Atabereka Serugi, Reu anakhalabe ndi moyo zaka zina 207. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 22  Serugi atakhala ndi moyo zaka 30, anabereka Nahori.+ 23  Atabereka Nahori, Serugi anakhalabe ndi moyo zaka zina 200. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 24  Nahori atakhala ndi moyo zaka 29, anabereka Tera.+ 25  Atabereka Tera, Nahori anakhalabe ndi moyo zaka zina 119. Pa zaka zimenezi, anabereka ana aamuna ndi aakazi. 26  Tera anakhala ndi moyo zaka 70, kenako anabereka Abulamu,+ Nahori+ ndi Harana. 27  Tsopano iyi ndi mbiri ya Tera. Tera anabereka Abulamu, Nahori ndi Harana. Harana anabereka Loti.+ 28  Pambuyo pake Harana anamwalira mumzinda wa Akasidi+ wa Uri,+ kumene anabadwira. Anamwalira bambo ake Tera adakali ndi moyo. 29  Abulamu ndi Nahori anakwatira. Mkazi wa Abulamu anali Sarai,+ pamene mkazi wa Nahori anali Milika,+ mwana wa Harana. Harana ameneyu analinso bambo ake a Yisika. 30  Koma Sarai anali wosabereka,+ choncho analibe mwana. 31  Pambuyo pake Tera anatenga mwana wake Abulamu, mdzukulu wake+ Loti mwana wa Harana, Sarai+ mpongozi wake, mkazi wa mwana wake Abulamu, ndi kunyamuka kuchoka mumzinda wa Akasidi wa Uri, kupita kudziko la Kanani.+ Kenako, anafika ku Harana+ ndipo anakhala kumeneko. 32  Choncho masiku a Tera anakwana zaka 205. Kenako, iye anamwalira ku Harana.

Mawu a M'munsi