Yobu 37:1-24
37 “Chifukwa cha zimenezi, mtima wanga ukugunda kwambiri,Ukungokhala ngati uchoka mʼmalo mwake.
2 Mvetserani mwatcheru mawu amphamvu a Mulungu,Komanso mabingu ochokera mʼkamwa mwake.
3 Amene amamveka pansi ponse pa thambo,Ndipo amatumiza mphezi yake+ kumalekezero a dziko lapansi.
4 Pambuyo pake pamamveka phokoso.Iye amabangula ndi mawu amphamvu,+Ndipo mphezi zimakhala zikuwala iye akamalankhula.
5 Mulungu amabangula ndi mawu ake+ mochititsa chidwi kwambiri.Amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.+
6 Chifukwa amauza matalala kuti, ‘Gwerani padziko lapansi,’+
Ndipo mvula amaiuza kuti, ‘Igwa mwamphamvu kwambiri.’+
7 Mulungu amaimitsa chilichonse chimene anthu akuchita,*Kuti munthu aliyense adziwe ntchito Yake.
8 Nyama zakutchire zimapita mʼnyumba zawo,Ndipo zimakhalabe mʼmalo amene zimakhala.
9 Mphepo yamkuntho imaomba kuchokera kumalo ake,+Ndipo kuzizira kumachokera mumphepo yakumpoto.+
10 Pogwiritsa ntchito mpweya wake Mulungu amapangitsa kuti madzi aundane,+Komanso kuti madzi aundane chifukwa cha kuzizira.+
11 Iye amachititsa kuti mitambo ilemedwe ndi chinyontho.Amamwaza mphezi+ zake mʼmitambo.
12 Mitamboyo imayenda mozungulira ndipo iye amailamula kuti ipite kumene akufuna.Imachita chilichonse chimene iye walamula+ panthaka yapadziko lapansi.*
13 Amagwiritsa ntchito mitamboyo kuti apereke chilango,*+ kuti anyowetse dziko,Komanso kuti asonyeze chikondi chokhulupirika.+
14 Mvetserani izi inu a Yobu,Imani ndi kuganizira mozama ntchito zodabwitsa za Mulungu.+
15 Kodi mukudziwa zimene Mulungu amachita kuti alamulire mitamboKomanso zimene amachita kuti mphezi ziziwala mʼmitambo yake?
16 Kodi mukudziwa chimene chimachititsa kuti mitambo izikhala mʼmalere?+
Zimenezi ndi ntchito zodabwitsa za Mulungu amene amadziwa chilichonse.+
17 Nʼchifukwa chiyani zovala zanu zimatentha,Pamene mphepo yakumʼmwera yachititsa dziko lapansi kuti likhale bata?+
18 Kodi inuyo limodzi ndi iyeyo mungatambasule kuthambo,+Nʼkukumenyamenya kuti kukhale kolimba ngati chitsulo chonyezimira?*
19 Tiuzeni zoti timuuze.Sitingathe kuyankha chifukwa tili mumdima.
20 Kodi auzidwe kuti ndikufuna kulankhula?
Kapena kodi munthu wina wanena zinazake zimene akufunika kuti auzidwe?+
21 Iwo sangathe nʼkomwe kuona kuwala,*Ngakhale kuti kuthambo nʼkowala,Mpaka mphepo itadutsa nʼkuchotsa mitambo.
22 Ulemerero wonyezimira ngati golide umachokera kumpoto.Ulemerero wa Mulungu+ ndi wochititsa mantha.
23 Wamphamvuyonse sitingathe kumumvetsa.+Iye ali ndi mphamvu zazikulu,+Ndipo sachita zinthu zosemphana ndi chilungamo+ chake komanso kulungama kwake kodabwitsa.+
24 Choncho anthu azimuopa.+
Chifukwa sakondera aliyense amene amadziona kuti ndi wanzeru.”*+
Mawu a M'munsi
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “amaika chidindo padzanja la munthu aliyense.”
^ Kapena kuti, “panthaka yachonde yapadziko lapansi.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “ngati chikwapu.”
^ Kapena kuti, “ngati galasi lachitsulo.”
^ Kumene ndi kuwala kwa dzuwa.
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “amene ali ndi mtima wanzeru.”

