Yobu 36:1-33

  • Elihu anatamanda Mulungu chifukwa cha mphamvu zake zopanda malire (1-33)

    • Anthu omvera zinthu zimawayendera bwino; anthu oipa amakanidwa (11-13)

    • ‘Kodi pali mphunzitsi winanso wofanana ndi Mulungu?’ (22)

    • Yobu ankayenera kulemekeza Mulungu (24)

    • “Mulungu ndi wamkulu kuposa mmene tikudziwira” (26)

    • Mulungu amalamulira mvula komanso mphezi (27-33)

36  Elihu anapitiriza kunena kuti:   “Ndilezereni mtima kwa kanthawi kochepa kuti ndifotokoze,Chifukwa ndidakali ndi mawu oti ndinene mʼmalo mwa Mulungu.   Ndifotokoza mwatsatanetsatane zimene ndikudziwa,Ndipo ndinena kuti amene anandipanga, ndi wachilungamo.+   Ndikunena zoona, mawu anga si onama.Amene amadziwa chilichonse+ akukuonani.   Inde, Mulungu ndi wamphamvu+ ndipo sakana munthu aliyense.Iye ali ndi mphamvu zazikulu zomvetsa zinthu.*   Iye sadzateteza moyo wa anthu oipa,+Koma amachitira chilungamo anthu amene ali pamavuto.+   Iye sasiya kuyangʼanitsitsa wolungama.+Amawaika kukhala mafumu,+ ndipo amalemekezeka mpaka kalekale.   Koma akamangidwa mʼmatangadza,Nʼkugwidwa ndi zingwe zamavuto,   Iye amawaululira zimene achita,Zimene alakwitsa chifukwa cha kunyada kwawo. 10  Iye amatsegula makutu awo kuti awapatse malangizoNdi kuwauza kuti asiye kuchita zoipa.+ 11  Akamamumvera komanso kumutumikira,Zinthu zidzawayendera bwino pa nthawi yonse ya moyo wawo,Ndipo moyo wawo udzakhala wosangalatsa.+ 12  Koma akapanda kumvera, adzaphedwa ndi lupanga*+Ndipo adzafa ali osadziwa zinthu. 13  Anthu oipa mtima* adzasunga chakukhosi. Iwo sapempha thandizo ngakhale Mulungu atawamanga. 14  Iwo amafa adakali ana,+Amakhala pakati pa mahule aamuna apakachisi moyo wawo wonse.+ 15  Koma Mulungu amapulumutsa anthu ovutika pa mavuto awo,Amatsegula makutu awo akamaponderezedwa. 16  Iye amakukokani mukatsala pangʼono kukumana ndi mavuto+Nʼkukupititsani pamalo otakasuka, opanda mavuto.+Patebulo panu pali chakudya chambiri chabwino chimene chimakusangalatsani.+ 17  Kenako mudzakhutira ndi chiweruzo chimene chidzaperekedwe kwa oipa.+Pa nthawi imene chiweruzo chidzaperekedwe komanso chilungamo chidzatsatiridwe. 18  Samalani kuti mkwiyo usakuchititseni zinthu mwanjiru,*+Ndipo musalole kuti akupatseni ziphuphu zambiri nʼkukusocheretsani. 19  Kodi kulira kwanu kopempha thandizoKapena kuyesetsa kwanu mwamphamvu kungakuthandizeni kuti musakumane ndi mavuto?+ 20  Musamalakelake kuti usiku ufike,Pamene anthu amasowa pamalo awo. 21  Samalani kuti musayambe kuchita zinthu zoipa,Musasankhe zimenezi mʼmalo mwa mavuto.+ 22  Pajatu Mulungu ali ndi mphamvu zapamwamba.Kodi pali mphunzitsi winanso wofanana naye? 23  Ndi ndani anauzapo Mulungu kuti chitani izi,+Kapena ndi ndani amene anamuuza kuti, ‘Zimene mwachitazi ndi zolakwikaʼ?+ 24  Kumbukirani kulemekeza ntchito zake,+Zimene anthu amazitchula munyimbo zawo.+ 25  Anthu onse aziona,Munthu amaziyangʼana ali patali. 26  Inde Mulungu ndi wamkulu kuposa mmene tikudziwira.+Palibe amene angawerenge* zaka zimene wakhala ndi moyo.+ 27  Iye amakoka madontho a madzi.+Madonthowo amasintha nʼkukhala nkhungu imene imapanga mvula, 28  Kenako mitambo imagwetsa mvula,+Imagwetsera aliyense madzi. 29  Kodi alipo amene angamvetse mmene mitambo anaitambasulira,Komanso kugunda kochokera mutenti yake?*+ 30  Onani mmene amaiwalitsira ndi mphenzi zake*+Ndipo amaphimba pansi pa nyanja* ndi madzi. 31  Pogwiritsa ntchito zimenezi, iye amapereka chakudya kwa anthu onse.Amawapatsa chakudya chochuluka.+ 32  Iye amafumbata mphezi mʼmanja mwake,Ndipo amailamula kuti ikagwere pamene akufuna.+ 33  Mabingu ake amanena za iye,Ngakhale ziweto zimadziwa amene akubwera.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Mphamvu za mtima wake nʼzazikulu.”
Kapena kuti, “ndi chida.”
Kapena kuti, “ampatuko.”
Kapena kuti, “kuwomba mʼmanja mwanjiru.”
Kapena kuti, “Nʼzosatheka kufufuza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mumsasa wake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kuwala kwake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mizu ya nyanja.”