Yesaya 41:1-29

  • Amene adzawagonjetse adzachokera kotulukira dzuwa (1-7)

  • Isiraeli anasankhidwa kuti akhale mtumiki wa Mulungu (8-20)

    • “Mnzanga Abulahamu” (8)

  • Milungu ina ndi yosathandiza (21-29)

41  “Zilumba inu, khalani chete* ndi kundimvetsera.Inu mitundu ya anthu, pezaninso mphamvu. Bwerani pafupi ndi ine, kenako mulankhule.+ Tiyeni tikumane ndipo ndikuweruzani.   Kodi ndi ndani amene wapatsa mphamvu winawake kuchokera kotulukira dzuwa,*+Amene wamuitana mwachilungamo kuti ayandikire kumapazi ake,*Kuti amupatse mitundu ya anthuNdiponso kuti amuchititse kuti agonjetse mafumu?+ Kodi ndi ndani amene amawasandutsa fumbi pogwiritsa ntchito lupanga lake,Ndipo ndi ndani amene amawabalalitsa ngati mapesi ouluzika ndi mphepo pogwiritsa ntchito uta wake?   Iye amawathamangitsa, amadutsa popanda chilichonse chomusokonezaMʼnjira zimene mapazi ake sanayambe adutsamo.   Ndi ndani wachita zimenezi,Ndi ndani waitana mibadwo kuchokera pachiyambi? Ndi ineyo Yehova, ndine Woyamba,+Ndipo kwa omalizira ndimakhala chimodzimodzi.”+   Zilumba zaona zimenezi ndipo zachita mantha. Malekezero a dziko lapansi anayamba kunjenjemera. Mitundu ya anthu inayandikira nʼkubwera.   Aliyense akuthandiza mnzakeNdipo akuuza mʼbale wake kuti: “Limba mtima.”   Choncho mmisiri wa mitengo akulimbikitsa mmisiri wa zitsulo.+Amene amawongola zitsulo ndi hamalaAkulimbikitsa munthu amene akusula zitsulo ndi hamala. Ponena za ntchito yowotcherera zitsulo ndi mtovu, iye akuti: “Zili bwino.” Kenako amakhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.   “Koma iwe Isiraeli, ndiwe mtumiki wanga,+Iwe Yakobo, amene ndakusankha,+Mbadwa* ya mnzanga Abulahamu.+   Iwe amene ndinakutenga kuchokera kumalekezero a dziko lapansi,+Ndiponso iwe amene ndinakuitana kuchokera kumadera akutali a dziko lapansi. Ndinakuuza kuti, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga.+Ndakusankha ndipo sindinakutaye.+ 10  Usachite mantha, chifukwa ndili ndi iwe.+ Usade nkhawa chifukwa ine ndine Mulungu wako.+ Ndikulimbitsa, ndithu ndikuthandiza,+Ndikugwira mwamphamvu ndi dzanja langa lamanja lachilungamo.’ 11  Taona! Onse amene amakupsera mtima adzachita manyazi ndipo adzanyozeka.+ Anthu amene akumenyana nawe adzawonongedwa ndipo adzatha.+ 12  Anthu amene akulimbana nawe udzawafunafuna koma sudzawapeza.Anthu amene akumenyana nawe adzakhala ngati chinthu chimene kulibeko ndipo sadzakhalanso ngati kanthu.+ 13  Chifukwa ine, Yehova Mulungu wako, ndagwira dzanja lako lamanja,Ine amene ndikukuuza kuti, ‘Usachite mantha. Ineyo ndikuthandiza.’+ 14  “Usachite mantha, nyongolotsi* iwe Yakobo,+Inu amuna a mu Isiraeli, ineyo ndikuthandizani,” akutero Yehova, Wokuwombolani,+ Woyera wa Isiraeli. 15  “Taona! Ndakusandutsa chopunthira mbewu,+Chida chatsopano chopunthira mbewu chokhala ndi mano akuthwa konsekonse. Udzapondaponda mapiri nʼkuwaphwanyaNdipo zitunda udzazisandutsa mankhusu. 16  Udzapeta mapiri ndi zitundazoNdipo mphepo idzaziuluza.Mphepo yamkuntho idzazimwaza. Iweyo udzasangalala chifukwa cha Yehova,+Ndipo udzadzitama chifukwa cha Woyera wa Isiraeli.”+ 17  “Anthu ovutika ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza. Lilime lawo lauma chifukwa cha ludzu.+ Ineyo Yehova ndidzawayankha.+ Ineyo Mulungu wa Isiraeli, sindidzawasiya.+ 18  Ndidzachititsa kuti mitsinje yamadzi iyende mʼmapiri opanda zomera zilizonse+Komanso kuti akasupe atuluke mʼzigwa.+ Chipululu ndidzachisandutsa dambo lamadziNdipo dziko lopanda madzi ndidzalisandutsa akasupe amadzi.+ 19  Mʼchipululu ndidzadzalamo mtengo wa mkungudza,Mtengo wa mthethe, mtengo wa mchisu ndi mtengo wa paini.+ Mʼchigwa chamʼchipululu ndidzadzalamo mtengo wa junipa,*Limodzi ndi mtengo wa ashi* komanso mtengo wofanana ndi mkungudza,+ 20  Ndidzachita zimenezi kuti anthu onse aone ndipo adziwe,Amve ndiponso azindikireKuti dzanja la Yehova ndi limene lachita zimenezi,Ndiponso kuti Woyera wa Isiraeli ndi amene wachititsa zimenezi.”+ 21  “Bweretsani kuno mlandu wanu,” akutero Yehova. “Fotokozani mfundo zanu,” ikutero Mfumu ya Yakobo. 22  “Tipatseni umboni ndipo mutiuze zinthu zimene zidzachitike. Tiuzeni zokhudza zinthu zakale,*Kuti tiziganizire mozama nʼkudziwa tsogolo lake. Kapena mutiuze zinthu zimene zikubwera.+ 23  Tiuzeni zinthu zimene zidzachitike mʼtsogolo,Kuti tidziwe kuti ndinu milungu.+ Inde, chitani chinachake, chabwino kapena choipa,Kuti tidabwe tikachiona.+ 24  Taonani! Inuyo ndi chinthu chopanda ntchito,Ndipo palibe chimene mwakwanitsa kuchita.+ Aliyense amene amasankha kukulambirani ndi wonyansa.+ 25  Ine ndapatsa mphamvu winawake kuchokera kumpoto, ndipo abwera.+Iye adzachokera kotulukira dzuwa*+ ndipo adzaitana pa dzina langa. Adzapondaponda olamulira* ngati akuponda dongo+Ngati woumba amene amapondaponda dongo laliwisi. 26  Kodi ndi ndani ananenapo zokhudza zimenezi kuchokera pachiyambi kuti tidziwe,Kapena kuchokera kalekale kuti tinene kuti, ‘Akunena zoonaʼ?+ Ndithu palibe amene analengeza zimenezi. Palibe amene ananena chilichonse. Palibe amene anamva chilichonse kuchokera kwa inu.”+ 27  Ine ndinali woyamba kuuza Ziyoni kuti: “Tamverani zimene zidzachitike!”+ Ndipo ku Yerusalemu ndidzatumizako munthu wobweretsa uthenga wabwino.+ 28  Koma ndinapitiriza kuyangʼana, ndipo panalibe aliyense.Pakati pa mafanowo panalibe aliyense amene akanapereka malangizo. Ndipo ndinapitiriza kuwafunsa, koma palibe anayankha. 29  Onsewo ndi opanda ntchito.* Ntchito zawo ndi zopanda pake. Mafano awo opangidwa ndi zitsulo* ali ngati mphepo ndipo ndi opanda ntchito.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “khalani chete pamaso panga.”
Kapena kuti, “kuchokera kumʼmawa.”
Kutanthauza kumutumikira.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mbewu.”
Kutanthauza wopanda chitetezo chilichonse komanso wonyozeka.
Mtengo wa junipa ndi wofanana ndi mtengo wa mkungudza.
Umenewu ndi mtengo waukulu umene umatalika mpaka mamita 15. Umakhala ndi masamba osabiriwira kwambiri ndi nthambi zotuwa ngati phulusa.
Mʼchilankhulo choyambirira, “zoyambirira.”
Kapena kuti, “kuchokera kumʼmawa.”
Kapena kuti, “achiwiri kwa olamulira.”
Kapena kuti, “ndi chinthu chimene kulibe.”
Kapena kuti, “zitsulo zosungunula.”