Yesaya 53:1-12

  • Kuvutika, imfa komanso kuikidwa mʼmanda kwa mtumiki wa Yehova (1-12)

    • Ananyozedwa komanso kupewedwa (3)

    • Ananyamula matenda ndi zowawa (4)

    • “Anamutengera kumalo oti akamuphere ngati nkhosa” (7)

    • Ananyamula tchimo la anthu ambiri  (12)

53  Kodi ndi ndani amene wakhulupirira zinthu zimene anamva kwa ife?*+ Ndipo kodi dzanja la Yehova+ laonetsedwa kwa ndani?+  2  Iye adzaphuka ngati nthambi+ pamaso pawinawake* ndiponso ngati muzu wotuluka mʼnthaka youma. Saoneka ngati munthu wapadera kapena waulemerero,+Ndipo tikamuona, maonekedwe ake si ochititsa chidwi moti ife nʼkukopeka naye.*  3  Iye ananyozedwa ndipo anthu ankamupewa,+Anali munthu amene kupweteka ankakudziwa bwino* ndipo matenda ankawadziwa. Zinali ngati kuti nkhope yake yabisika kwa ife.* Ananyozedwa ndipo tinkamuona ngati wopanda pake.+  4  Zoonadi, iye ananyamula matenda athu,+Ndipo anasenza zowawa zathu.+ Koma ifeyo tinkamuona ngati munthu amene wagwidwa ndi matenda, amene walangidwa* ndi Mulungu ndiponso kuzunzidwa.  5  Koma iye anabayidwa+ chifukwa cha zolakwa zathu.+Anaphwanyidwa chifukwa cha zochimwa zathu.+ Analandira chilango kuti ife tikhale pamtendere,+Ndipo chifukwa cha mabala ake ifeyo tinachiritsidwa.+  6  Tonsefe tikungoyendayenda uku ndi uku ngati nkhosa zosochera.+Aliyense akulowera njira yakeNdipo Yehova wachititsa kuti zolakwa za tonsefe zigwere pa ameneyo.+  7  Iye anachitiridwa zankhanza+ ndipo analola kuti azunzidwe,+Koma sanatsegule pakamwa pake. Anamutengera kumalo oti akamuphere ngati nkhosa,+Mofanana ndi nkhosa yaikazi imene yangokhala chete pamene akufuna kuimeta ubweya,Ndipo sanatsegule pakamwa pake.+  8  Iye anaponderezedwa ndipo anatengedwa popanda kuweruzidwa mwachilungamo.Ndi ndani amene anaganizira tsatanetsatane wa mʼbadwo wa makolo ake?* Popeza iye anadulidwa mʼdziko la anthu amoyo.+Iye anakwapulidwa* chifukwa cha zolakwa za anthu anga.+  9  Anapatsidwa manda* limodzi ndi anthu oipa,+Ndipo pamene anafa anaikidwa mʼmanda limodzi ndi anthu olemera,*+Ngakhale kuti iye sanalakwe chilichonse*Ndipo mʼkamwa mwake munalibe chinyengo.+ 10  Koma Yehova ndi amene anafuna* kuti mtumiki wake aphwanyidwe ndipo anamulola kuti adwale. Ngati mungapereke moyo wake kuti ukhale nsembe yakupalamula,+Iye adzaona ana ake,* adzakhala ndi moyo kwa nthawi yaitali,+Ndipo kudzera mwa iye, zofuna za* Yehova zidzatheka.+ 11  Chifukwa cha kuvutika kwake, iye adzaona zabwino ndipo adzakhutira. Chifukwa cha zimene mtumiki wanga wolungama akudziwa,+Adzachititsa kuti anthu ambiri azionedwa olungama,+Ndipo adzanyamula zolakwa zawo.+ 12  Pa chifukwa chimenechi, ndidzamupatsa gawo pamodzi ndi ambiri,Ndipo iye adzagawana ndi amphamvu katundu amene alanda kunkhondo,Chifukwa anapereka moyo wake*+Ndipo anaikidwa mʼgulu la anthu ochimwa.+Ananyamula tchimo la anthu ambiri+Ndipo analowererapo kuti athandize anthu ochimwa.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “zimene ife tinamva.”
“Winawake” angaimire munthu wina amene akungoonerera kapena Mulungu.
Kapena kuti, “saoneka mwapadera moti nʼkumusirira.”
Kapena kuti, “amene ankamvetsa kuti kupweteka nʼchiyani.”
Mabaibulo ena amati, “Anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amene wakwapulidwa.”
Kapena kuti, “wa zochitika pa moyo wake.”
Kapena kuti, “anamenyedwa mpaka kufa.”
Kapena kuti, “Ndipo wina adzapereka manda ake.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “munthu wolemera.”
Kapena kuti, “sanachite zachiwawa.”
Kapena kuti, “zimene zimasangalatsa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mbewu zake.”
Kapena kuti, “Koma zinamukomera Yehova.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anakhuthula moyo wake mu imfa.”