Ekisodo 11:1-10

  • Ananena za mliri wa 10 (1-10)

    • Aisiraeli anapempha mphatso (2)

11  Choncho Yehova anauza Mose kuti: “Patsala mliri umodzi wokha woti ndigwetsere Farao ndi Iguputo. Kenako adzakulolani kuchoka mʼdziko lino.+ Pokuuzani kuti muchoke, adzachita kukuthamangitsani.+ 2  Tsopano uza anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa munthu wokhala naye pafupi zinthu zasiliva ndi zagolide.”+ 3  Ndiyeno Yehova anachititsa kuti Aiguputo akomere mtima Aisiraeli. Komanso Mose ankalemekezedwa kwambiri mʼdziko la Iguputo, pamaso pa atumiki a Farao ndi pamaso pa Aiguputo onse. 4  Choncho Mose anati: “Yehova wanena kuti, ‘Pakati pa usiku ndilowa mu Iguputo,+ 5  ndipo mwana aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Iguputo adzafa.+ Kuyambira mwana woyamba wa Farao amene wakhala pampando wachifumu, mpaka mwana woyamba wa kapolo wamkazi amene akugwira ntchito pamphero* ndiponso mwana woyamba kubadwa wa nyama iliyonse.+ 6  Mʼdziko lonse la Iguputo mudzakhala kulira kwakukulu kumene sikunachitikepo ndiponso kumene sikudzachitikanso.+ 7  Ngakhale galu sadzauwa aliyense wa Aisiraeli, sadzauwa anthu kapena ziweto zawo, kuti mudziwe kuti Yehova akhoza kuchitira Aisiraeli zinthu zosiyana ndi zimene angachitire Aiguputo.’+ 8  Ndipo atumiki anu onsewa adzabwera kwa ine nʼkundigwadira komanso kundiweramira. Iwo adzanena kuti, ‘Pita, iweyo ndi anthu onse amene amakutsatira.’+ Akadzatero ndidzapitadi.” Atanena mawu amenewa anachoka kwa Farao atakwiya. 9  Kenako Yehova anauza Mose kuti: “Farao sadzakumverani inu.+ Izi zili choncho kuti ndichite zodabwitsa zochuluka mʼdziko la Iguputo.”+ 10  Mose ndi Aroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao.+ Koma Yehova analola Farao kuumitsa mtima wake, moti sanalole kuti Aisiraeli achoke mʼdziko lake.+

Mawu a M'munsi

“Mphero” ndi mwala umene ankaugwiritsa ntchito popera mbewu kuti apange ufa.