Mika 4:1-13
4 Mʼmasiku otsiriza,Phiri la nyumba ya Yehova+Lidzakhazikika pamwamba penipeni pa mapiri akuluakulu,Ndipo lidzakwezedwa kupitirira mapiri angʼonoangʼono.Anthu a mitundu yosiyanasiyana adzapita kumeneko.+
2 Anthu ochokera mʼmitundu yosiyanasiyana adzabwera nʼkunena kuti:
“Bwerani, tiyeni tipite kuphiri la Yehova,Tipite kunyumba ya Mulungu wa Yakobo.+
Iye akatiphunzitsa njira zake,Ndipo ife tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Chifukwa chilamulo,* chidzaphunzitsidwa mu ZiyoniNdipo mawu a Yehova adzaphunzitsidwa mu Yerusalemu.
3 Mulungu adzaweruza mitundu yambiri ya anthu,+Ndipo adzakonza zinthu zolakwika zokhudza anthu ochokera mʼmitundu yamphamvu yakutali.
Iwo adzasula malupanga awo kuti akhale makasu a pulawo,Ndiponso mikondo yawo kuti ikhale zida zosadzira mitengo.+
Mtundu wa anthu sudzanyamula lupanga kuti umenyane ndi mtundu unzake,Ndipo anthuwo sadzaphunziranso nkhondo.+
4 Aliyense adzakhala pansi pa mtengo wake wa mpesa ndi mtengo wake wa mkuyu,+Ndipo sipadzakhala wowaopseza,+Chifukwa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena zimenezi.
5 Anthu a mtundu uliwonse adzayenda mʼdzina la mulungu wawo.Koma ife tidzayenda mʼdzina la Yehova Mulungu+ wathu mpaka kalekale.
6 Yehova wanena kuti, “Pa tsiku limenelo,Ndidzasonkhanitsa anthu amene ankayenda motsimphina.Ndidzasonkhanitsanso anthu amene anamwazikana,+Komanso anthu amene ndinawalanga.
7 Anthu amene ankayenda motsimphina, ndidzawasonkhanitsanso ngati anthu otsala.+Anthu amene anachotsedwa mʼdziko lawo nʼkupita kutali, ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.+Ndipo Yehova adzakhala mfumu yawo mʼphiri la Ziyoni,Kuyambira panopa mpaka kalekale.
8 Koma iwe nsanja ya gulu la nkhosa,Malo okwera a mwana wamkazi wa Ziyoni,*+Ulamuliro udzabwerera. Ulamuliro woyamba udzabwerera kwa iwe,+Ufumu wa mwana wamkazi wa Yerusalemu.*+
9 Ndiye nʼchifukwa chiyani ukufuula kwambiri?
Kodi ulibe mfumu?Kapena alangizi ako awonongedwa?Moti ukumva zowawa ngati mkazi amene akubereka?+
10 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni udzamva ululu woopsa,Ngati mkazi amene akubereka.Chifukwa tsopano uchoka mʼtauni nʼkupita kukakhala kumudzi.
Ukafika mpaka ku Babulo,+Ndipo kumeneko udzapulumutsidwa.+Kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.+
11 Anthu amitundu yosiyanasiyana adzasonkhana kuti akuukire.Anthuwo adzanena kuti, ‘Tiyeni timuwononge,Ndipo maso athu aone zimenezi zikuchitikira Ziyoni.’
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova.Iwo sakumvetsa cholinga chake.Chifukwa adzawasonkhanitsa pamalo opunthira mbewu ngati mmene amasonkhanitsira tirigu amene angomumweta kumene.
13 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, nyamuka upunthe tirigu.+Chifukwa nyanga zako ndidzazisandutsa chitsulo.Ziboda zako ndidzazisandutsa kopa.*Ndipo udzanyenyanyenya mitundu yambiri ya anthu.+
Phindu limene iwo apeza mwachinyengo, udzalipereka kwa Yehova.Ndipo zinthu zawo udzazipereka kwa Ambuye woona wa dziko lonse lapansi.”+
Mawu a M'munsi
^ Kapena kuti, “malangizo.”
^ Mawu akuti “mwana wamkazi wa Ziyoni” ndi mawu andakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Yerusalemu kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.
^ Mawu akuti “mwana wamkazi wa Yerusalemu” ndi mawu andakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Yerusalemu kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.
^ Kapena kuti, “mkuwa.”