Mateyu 7:1-29

7  “Lekani kuweruza ena+ kuti inunso musaweruzidwe,  pakuti chiweruzo chimene mukuweruza nacho ena inunso mudzaweruzidwa nacho.+ Ndipo muyezo umene mukuyezera ena, iwonso adzakuyezerani womwewo.+  Nanga n’chifukwa chiyani umayang’ana kachitsotso m’diso la m’bale wako, koma osaganizira mtanda wa denga* la nyumba umene uli m’diso lako?+  Kapena ungauze bwanji m’bale wako kuti, ‘Taima ndikuchotse kachitsotso m’diso lako,’ pamene iwe m’diso lako muli mtanda wa denga la nyumba?+  Wonyenga iwe! Yamba wachotsa mtanda wa denga la nyumba uli m’diso lakowo, ndipo ukatero udzatha kuona bwino mmene ungachotsere kachitsotso m’diso la m’bale wako.  “Musamapatse agalu zinthu zopatulika,+ kapena kuponyera nkhumba ngale zanu, kuopera kuti zingapondeponde ngalezo+ kenako n’kutembenuka ndi kukukhadzulani.  “Pemphanibe,+ ndipo adzakupatsani. Pitirizani kufunafuna, ndipo mudzapeza. Gogodanibe,+ ndipo adzakutsegulirani.  Pakuti aliyense wopempha amalandira,+ aliyense wofunafuna amapeza, ndipo aliyense wogogoda adzamutsegulira.  Inde, ndani pakati panu amene mwana wake+ atamupempha mkate, iye angamupatse mwala? 10  Kapena atamupempha nsomba, kodi angamupatse njoka? 11  Chotero ngati inuyo, ngakhale kuti ndinu oipa,+ mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, kuli bwanji Atate wanu wakumwamba? Ndithudi, iye adzapereka zinthu zabwino+ kwa onse om’pempha! 12  “Zinthu zonse zimene mukufuna kuti anthu akuchitireni,+ inunso muwachitire zomwezo, pakuti n’zimene Chilamulo ndi Zolemba za aneneri zimafuna.+ 13  “Lowani pachipata chopapatiza.+ Pakuti msewu waukulu ndi wotakasuka ukupita kuchiwonongeko, ndipo anthu ambiri akuyenda mmenemo. 14  Koma chipata cholowera ku moyo n’chopapatiza komanso msewu wake ndi wopanikiza, ndipo amene akuupeza ndi owerengeka.+ 15  “Chenjerani ndi aneneri onyenga+ amene amabwera kwa inu atavala ngati nkhosa,+ koma mkati mwawo ali mimbulu yolusa.+ 16  Mudzawazindikira ndi zipatso zawo.+ Anthu sathyola mphesa paminga kapena nkhuyu pamitula, amatero kodi?+ 17  Momwemonso mtengo uliwonse wabwino umabala zipatso zabwino, koma mtengo uliwonse wovunda umabala zipatso zopanda pake.+ 18  Mtengo wabwino sungabale zipatso zopanda pake, ndiponso mtengo wovunda sungabale zipatso zabwino. 19  Mtengo uliwonse wosabala zipatso zabwino amaudula ndi kuuponya pamoto.+ 20  Chotero anthu amenewo mudzawazindikira ndi zipatso zawo.+ 21  “Sikuti aliyense wonena kwa ine kuti, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowa ufumu wakumwamba ayi, koma yekhayo amene akuchita+ chifuniro cha Atate wanga wakumwamba.+ 22  Ambiri adzati kwa ine pa tsiku limenelo, ‘Ambuye, Ambuye,+ kodi ife sitinalosere m’dzina lanu, ndi kutulutsa ziwanda m’dzina lanu, ndiponso kuchita ntchito zambiri zamphamvu m’dzina lanunso?’+ 23  Koma ine ndidzawauza momveka bwino kuti: Sindikukudziwani ngakhale pang’ono!+ Chokani pamaso panga, anthu osamvera malamulo inu.+ 24  “Chotero aliyense wakumva mawu angawa ndi kuwachita adzafanizidwa ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe.+ 25  Ndiyeno kunagwa chimvula champhamvu ndipo madzi anasefukira. Kenako chimphepo chinafika n’kuwomba nyumbayo, koma sinagwe chifukwa chakuti inakhazikika pathanthwepo. 26  Aliyense wakumva mawu angawa koma osawachita+ adzafanizidwa ndi munthu wopusa+ amene anamanga nyumba yake pamchenga. 27  Ndiye kunagwa chimvula champhamvu ndipo madzi anasefukira. Kenako chimphepo chinafika n’kuwomba nyumbayo+ moti inagwa, ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”+ 28  Tsopano Yesu atatsiriza mawu amenewa, khamu la anthulo linakhudzidwa moti linadabwa+ ndi kaphunzitsidwe kake, 29  chifukwa anali kuwaphunzitsa monga munthu waulamuliro,+ osati monga alembi awo.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti “tsindwi.”