Mateyu 26:1-75

26  Tsopano Yesu atatsiriza kunena mawu onsewa, anauza ophunzira ake kuti:  “Inu mukudziwa kuti pasika achitika pakangopita masiku awiri,+ ndipo Mwana wa munthu aperekedwa kuti akapachikidwe.”+  Pa nthawiyi, ansembe aakulu ndiponso akulu anasonkhana m’bwalo lamkati kunyumba ya mkulu wa ansembe wotchedwa Kayafa.+  Iwo anali kupangana+ zoti agwire Yesu mochenjera ndi kumupha.  Koma anali kumangonena kuti: “Tisadzamugwire pa chikondwerero, kuopera kuti anthu angadzachite chipolowe.”+  Pamene Yesu anali ku Betaniya+ m’nyumba ya Simoni wakhate,+  kunafika mayi wina ndi botolo lopangidwa ndi mwala wa alabasitala muli mafuta onunkhira okwera mtengo.+ Mayiyo atayandikira Yesu, anayamba kumuthira mafutawo m’mutu pamene iye anali kudya patebulo.  Ophunzira ake ataona zimenezi anakwiya n’kunena kuti: “N’kuwonongeranji chonchi?+  Mafuta amenewa akanagulitsidwa ndalama zambiri ndipo ndalamazo zikanaperekedwa kwa anthu osauka.”+ 10  Yesu anadziwa zimenezi,+ ndipo anawafunsa kuti: “N’chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Iyetu wandichitira zinthu zabwino.+ 11  Osaukawo muli nawo nthawi zonse,+ koma ine simudzakhala nane nthawi zonse.+ 12  Pakuti pamene mayiyu wathira mafuta onunkhirawa pathupi langa chonchi, wachita zimenezi kukonzekera kuikidwa kwanga m’manda.+ 13  Ndithu ndikukuuzani, Kulikonse kumene uthenga wabwinowu udzalalikidwe m’dziko lonse, anthu azidzanena zimene mayiyu wachita kuti azidzam’kumbukira.”+ 14  Pambuyo pake mmodzi wa ophunzira 12 aja, wotchedwa Yudasi Isikariyoti,+ anapita kwa ansembe aakulu 15  n’kuwafunsa kuti: “Kodi mudzandipatsa chiyani ndikamupereka kwa inu?”+ Iwo anamulonjeza ndalama 30 zasiliva.+ 16  Choncho kuchokera pamenepo anayesetsa kufunafuna mpata wabwino umene angamuperekere.+ 17  Pa tsiku loyamba la chikondwerero cha mikate yopanda chofufumitsa,+ ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti: “Kodi mukufuna tikakukonzereni kuti malo odyerako pasika?”+ 18  Iye anati: “Pitani mumzinda kwa Munthu wakutiwakuti+ ndipo mukamuuze kuti, Mphunzitsi wanena kuti, ‘Nthawi yanga yoikidwiratu yayandikira. Ndidzachita phwando la pasika pamodzi ndi ophunzira anga kunyumba kwako.’”+ 19  Chotero ophunzirawo anachitadi monga mmene Yesu anawalamulira, ndipo anakonza zinthu zonse zofunika pa pasika.+ 20  Nthawi yamadzulo,+ iye ndi ophunzira ake 12 aja anali kudya chakudya patebulo.+ 21  Pamene anali kudya, iye anati: “Ndithu ndikukuuzani, Mmodzi wa inu andipereka.”+ 22  Chifukwa chomva chisoni kwambiri ndi zimenezi, aliyense anayamba kumufunsa kuti: “Ambuye, kodi ndine kapena?”+ 23  Poyankha iye anati: “Amene akusunsa nane limodzi m’mbalemu ndi amene ati andipereke.+ 24  Zoona, Mwana wa munthu akuchokadi, monga Malemba amanenera+ za iye, koma tsoka+ kwa munthu amene akupereka Mwana wa munthu!+ Zikanakhala bwino munthu ameneyu akanapanda kubadwa.” 25  Poyankha, Yudasi amene anali atatsala pang’ono kumupereka anati: “Nanga n’kukhala ine Rabi?” Iye anati: “Wanena wekha.” 26  Pamene anali kudya, Yesu anatenga mkate,+ ndipo atapempha dalitso, anaunyemanyema+ n’kuupereka kwa ophunzira ake. Iye anati: “Eni, idyani. Mkate uwu ukuimira thupi langa.”+ 27  Kenako anatenga kapu+ ndipo atayamika, anaipereka kwa iwo n’kunena kuti: “Imwani nonsenu.+ 28  Vinyoyu akuimira+ ‘magazi+ anga a pangano,’+ amene adzakhetsedwa chifukwa cha anthu ambiri+ kuti machimo akhululukidwe.+ 29  Koma ndikukuuzani kuti, kuyambira tsopano sindidzamwanso chakumwa ichi chochokera ku mphesa kufikira tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano limodzi ndi inu mu ufumu wa Atate wanga.”+ 30  Potsirizira pake, atatha kuimba nyimbo zotamanda Mulungu,+ anatuluka n’kupita kuphiri la Maolivi.+ 31  Kenako Yesu anawauza kuti: “Nonsenu muthawa ndi kundisiya ndekha usiku uno, pakuti Malemba amati, ‘Ndidzapha m’busa, ndipo nkhosa za m’gululo zidzabalalika.’+ 32  Koma ndikadzauka kwa akufa, ndidzatsogola kukafika ku Galileya inu musanafikeko.”+ 33  Koma Petulo anamuyankha kuti: “Ngakhale ena onse atathawa kukusiyani, ine ndekha sindingathawe!”+ 34  Yesu anamuuza kuti: “Ndithu ndikukuuza iwe, Usiku womwe uno tambala asanalire, undikana katatu.”+ 35  Petulo anayankha kuti: “Ngati kuli kufa, ine ndifa nanu limodzi, sindingakukaneni.” Ophunzira ena onse ananenanso chimodzimodzi.+ 36  Kenako Yesu anafika nawo pamalo+ otchedwa Getsemane, ndipo anauza ophunzirawo kuti: “Khalani pansi pompano, ine ndikupita uko kukapemphera.”+ 37  Popita kumeneko anatenga Petulo ndi ana awiri+ a Zebedayo. Ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika kwambiri mumtima mwake.+ 38  Kenako anawauza kuti: “Moyo wanga ukumva chisoni chofa nacho.+ Khalani pompano ndipo mukhalebe maso pamodzi ndi ine.”+ 39  Choncho atapita patsogolo pang’ono, anagwada mpaka nkhope yake pansi, ndipo anapemphera+ kuti: “Atate wanga, ngati n’kotheka, kapu+ iyi indipitirire. Koma osati mwa kufuna kwanga,+ koma mwa kufuna kwanu.”+ 40  Atatero anabwerera pamene panali ophunzira ake aja ndipo anawapeza akugona. Choncho anafunsa Petulo kuti: “Zoona anthu inu simungathe kukhalabe maso limodzi ndi ine ola limodzi?+ 41  Khalani maso+ ndipo pempherani+ kosalekeza kuti musalowe m’mayesero.+ Zoona, mzimu ndi wofunitsitsa, koma thupi ndi lofooka.”+ 42  Anachokanso kachiwiri+ n’kupita kukapemphera kuti: “Atate wanga, ngati sizingatheke kuti kapuyi indipitirire mpaka nditamwa ndithu, chifuniro chanu chichitike.”+ 43  Anabwerera n’kuwapezanso akugona, chifukwa zikope zawo zinali zitalemera.+ 44  Choncho anawasiya ndi kupitanso kukapemphera kachitatu,+ kubwereza mawu omwe aja. 45  Pambuyo pake anabwerera kwa ophunzirawo n’kuwauza kuti: “Zoona nthawi ngati ino mukugona ndi kupumula! Taonani! Ola lakuti Mwana wa munthu aperekedwe m’manja mwa ochimwa layandikira.+ 46  Nyamukani, tiyeni tizipita. Onani! Wondipereka uja ali pafupi.”+ 47  Mawu adakali m’kamwa, Yudasi,+ mmodzi wa ophunzira 12 aja, anafika limodzi ndi khamu lalikulu la anthu kuchokera kwa ansembe aakulu ndi kwa akulu, atanyamula malupanga+ ndi zibonga.+ 48  Apa n’kuti womupereka ameneyu atawapatsa chizindikiro chakuti: “Amene ndim’psompsone ndi ameneyo, mum’gwire.”+ 49  Atafika, Yudasi analunjika kwa Yesu n’kunena kuti: “Mtendere ukhale nanu Rabi!”+ Ndipo anam’psompsona.+ 50  Koma Yesu+ anamufunsa kuti: “Bwanawe, ukupezeka kuno ndi cholinga chotani?” Nthawi yomweyo iwo anayandikira ndipo anagwira Yesu ndi kum’manga.+ 51  Koma wina mwa amene anali ndi Yesu anasolola lupanga lake n’kutema nalo kapolo wa mkulu wa ansembe mpaka kuduliratu khutu lake.+ 52  Pamenepo Yesu anamuuza kuti: “Bwezera lupanga lako m’chimake,+ pakuti onse ogwira lupanga adzafa ndi lupanga.+ 53  Kapena ukuganiza kuti sindingapemphe Atate wanga kuti anditumizire magulu ankhondo oposa 12 a angelo nthawi yomwe ino?+ 54  Koma ndikachita zimenezo, nanga Malemba amene ananeneratu kuti izi ziyenera kuchitika adzakwaniritsidwa bwanji?” 55  Mu ola lomwelo Yesu anafunsa khamu la anthulo kuti: “Bwanji mwabwera kudzandigwira mutatenga malupanga ndi zibonga ngati mukukalimbana ndi wachifwamba?+ Tsiku ndi tsiku ndinali kukhala pansi m’kachisi+ ndi kuphunzitsa, koma simunandigwire. 56  Koma zonsezi zachitika kuti malemba a aneneri akwaniritsidwe.”+ Kenako ophunzira ake onse anamuthawa, n’kumusiya yekha.+ 57  Amene anagwira Yesu aja anapita naye kwa Kayafa+ mkulu wa ansembe, kumene alembi ndi akulu anali atasonkhana.+ 58  Koma Petulo anali kumutsatirabe chapatali ndithu, mpaka anafika m’bwalo lamkati+ kunyumba ya mkulu wa ansembeyo. Atalowa mkatimo, anakhala pansi pamodzi ndi antchito a m’nyumbamo kuti aone zotsatira zake.+ 59  Pa nthawiyi ansembe aakulu ndi Khoti lonse Lalikulu la Ayuda* anali kufunafuna umboni wonama kuti amunamizire mlandu Yesu ndi kumupha+ 60  koma sanaupeze, ngakhale kuti kunabwera mboni zambiri zonama.+ Patapita nthawi, kunabwera mboni zina ziwiri 61  ndi kunena kuti: “Munthu ameneyu ananena kuti, ‘Ndikhoza kugwetsa kachisi wa Mulungu ndi kumumanganso m’masiku atatu.’”+ 62  Pamenepo mkulu wa ansembe anaimirira ndi kumufunsa kuti: “Kodi ukusowa choyankha? Kodi n’zoona zimene awa akukunenezazi?”+ 63  Koma Yesu anangokhala chete.+ Chotero mkulu wa ansembe anati: “Ndikukulumbiritsa pali Mulungu wamoyo,+ utiuze ngati ndiwedi Khristu+ Mwana wa Mulungu!” 64  Yesu anamuyankha+ kuti: “Mwanena nokha.+ Ndipo ndikukuuzani anthu inu kuti, kuyambira tsopano+ mudzaona Mwana wa munthu+ atakhala kudzanja lamanja+ lamphamvu. Mudzamuonanso akubwera pamitambo yakumwamba.”+ 65  Pamenepo mkulu wa ansembe anang’amba malaya ake akunja n’kunena kuti: “Wanyoza Mulungu!+ Nanga n’kufunanso mboni zina pamenepa?+ Pano mwadzimvera nokha mmene akunyozera Mulungu.+ 66  Tsopano inu mukuona bwanji pamenepa?” Iwo anayankha kuti: “Ayenera kuphedwa basi.”+ 67  Kenako anayamba kumulavulira kunkhope+ ndi kum’menya+ nkhonya. Ena anamuwomba mbama,+ 68  ndi kunena kuti: “Losera tione Khristu iwe.+ Wakumenya ndani?”+ 69  Tsopano Petulo anakhala pansi m’bwalo lamkati, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye n’kunena kuti: “Inunso munali ndi Yesu wa ku Galileyayu!”+ 70  Koma iye anakana pamaso pa onse kuti: “Sindikudziwa zimene ukunena.” 71  Atatuluka n’kupita kukanyumba kapachipata, mtsikana wina anamuzindikira ndi kuuza ena amene anali pafupi kuti: “Bambo awa anali limodzi ndi Yesu Mnazaretiyu.”+ 72  Apanso Petulo anakana mochita kulumbira ndipo ananena kuti: “Ndithudi munthu ameneyu ine sindikumudziwa ayi!”+ 73  Patapita kanthawi pang’ono, amene anali ataimirira chapafupi anabwera ndi kuuza Petulo kuti: “Ndithu iwenso uli m’gulu la ophunzira ake. Ndipo kalankhulidwe kako kakugwiritsa.”+ 74  Pamenepo iye anayamba kutemberera ndi kulumbira kuti: “Munthu ameneyu ine sindikumudziwa ayi!” Nthawi yomweyo tambala analira.+ 75  Tsopano Petulo anakumbukira mawu a Yesu aja, akuti: “Tambala asanalire, udzandikana katatu.”+ Ndipo anatuluka panja n’kuyamba kulira mopwetekedwa mtima kwambiri.+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “Sanihedirini.”