Mateyu 22:1-46

22  Popitiriza kuwayankha, Yesu anawauzanso mafanizo ena kuti:+  “Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonza phwando la ukwati+ wa mwana wake.  Ndipo inatuma akapolo ake kuti akaitane anthu oitanidwa ku phwando laukwati,+ koma anthuwo sanafune kubwera.+  Kenako inatumanso akapolo ena+ kuti, ‘Kauzeni oitanidwawo kuti: “Ine ndakonza chakudya chamasana,+ ng’ombe zanga komanso nyama zanga zonenepa zaphedwa, ndipo zinthu zonse zakonzedwa kale. Bwerani ku phwando laukwati.”’+  Koma anthuwo ananyalanyaza ndi kuchoka. Wina anapita kumunda wake, wina kumalonda ake.+  Koma enawo anagwira akapolo akewo, ndi kuwachitira zachipongwe n’kuwapha.+  “Pamenepo mfumu ija inakwiya kwambiri, ndipo inatumiza asilikali ake kukawononga opha anthu amenewo ndi kutentha mzinda wawo.+  Kenako anauza akapolo ake kuti, ‘Phwando laukwati ndiye lakonzedwa ndithu, koma oitanidwa aja anali osayenera.+  Chotero pitani m’misewu yotuluka mumzinda, ndipo aliyense amene mukam’peze, mukamuitanire phwando laukwatili.’+ 10  Choncho akapolowo anapita m’misewu ndi kusonkhanitsa onse amene anawapeza, oipa ndi abwino omwe.+ Ndipo chipinda chodyeramo phwando laukwati chinadzaza ndi anthu oyembekezera kulandira chakudya.+ 11  “Pamene mfumu ija inalowa kukayendera alendowo, inaona munthu wina mmenemo amene sanavale chovala chaukwati.+ 12  Chotero inamufunsa kuti, ‘Bwanawe! Walowa bwanji muno usanavale chovala cha ukwati?’+ Iye anasowa chonena. 13  Kenako mfumuyo inauza atumiki ake kuti, ‘M’mangeni manja ndi miyendo ndipo mum’ponye kunja kumdima. Kumeneko akalira ndi kukukuta mano.’+ 14  “Pakuti oitanidwa ndi ambiri, koma osankhidwa ndi owerengeka.”+ 15  Pamenepo Afarisi anachoka ndi kukapangana kuti am’kole m’mawu ake.+ 16  Choncho anamutumizira ophunzira awo, limodzi ndi achipani cha Herode,+ ndipo iwo anati: “Mphunzitsi, tikudziwa kuti inu mumanena zoona ndipo mumaphunzitsa njira ya Mulungu m’choonadi, ndiponso simusamala kuti uyu ndani, chifukwa simuyang’ana maonekedwe a anthu.+ 17  Ndiye tatiuzani, Mukuganiza bwanji? Kodi n’kololeka kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”+ 18  Koma Yesu, podziwa kuipa mtima kwawo, ananena kuti: “Onyenga inu! Bwanji mukundiyesa?+ 19  Ndionetseni khobidi la msonkho.” Pamenepo anam’bweretsera khobidi limodzi la dinari. 20  Ndiyeno anawafunsa kuti: “Kodi nkhope iyi ndi mawu akewa n’zandani?”+ 21  Iwo anayankha kuti: “Ndi za Kaisara.” Pamenepo iye anawauza kuti: “Ndiye perekani zinthu za Kaisara kwa Kaisara, koma za Mulungu, kwa Mulungu.”+ 22  Atamva zimenezi, anadabwa ndipo anangochokapo n’kumusiya.+ 23  Pa tsikulo Asaduki, amene amanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa iye n’kumufunsa kuti:+ 24  “Mphunzitsi, Mose anati, ‘Ngati munthu wamwalira wopanda ana, m’bale wake ayenera kukwatira mkazi wamasiyeyo ndi kuberekera m’bale wake uja ana.’+ 25  Tsopano panali amuna 7 apachibale. Woyamba anakwatira kenako n’kumwalira. Koma popeza kuti analibe ana, mkazi uja anakwatiwa ndi m’bale wa mwamuna wake.+ 26  Zinachitika chimodzimodzi kwa wachiwiri ndi wachitatu, mpaka kwa onse 7 aja.+ 27  Pamapeto pake mkaziyo nayenso anamwalira. 28  Kodi pamenepa, pouka kwa akufa, mkazi ameneyu adzakhala wa ndani popeza onse 7 anamukwatira?”+ 29  Koma Yesu anawayankha kuti: “Mukulakwitsa chifukwa simudziwa Malemba kapena mphamvu ya Mulungu.+ 30  Pakuti pouka kwa akufa, amuna sadzakwatira ndipo akazi sadzakwatiwa,+ koma adzakhala ngati angelo akumwamba. 31  Kunena za kuuka kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,+ 32  ‘Ine ndine Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo’?+ Iye ndi Mulungu wa anthu amoyo, osati akufa.”+ 33  Pakumva zimenezo, khamu la anthulo linadabwa ndi zimene anali kuphunzitsa.+ 34  Afarisi atamva kuti Yesu anawasowetsa chonena Asaduki, anasonkhana monga gulu limodzi. 35  Ndipo mmodzi wa iwo, wodziwa Chilamulo,+ anafunsa Yesu momuyesa kuti: 36  “Mphunzitsi, kodi lamulo lalikulu kwambiri m’Chilamulo ndi liti?”+ 37  Iye anamuyankha kuti: “‘Uzikonda Yehova* Mulungu wako ndi mtima wako wonse, moyo wako wonse, ndi maganizo ako onse.’+ 38  Limeneli ndilo lamulo lalikulu kwambiri komanso loyamba. 39  Lachiwiri lofanana nalo ndi ili, ‘Uzikonda mnzako mmene umadzikondera wekha.’+ 40  Chilamulo chonse chagona pa malamulo awiri amenewa, kuphatikizaponso Zolemba za aneneri.”+ 41  Tsopano Afarisi aja atasonkhana pamodzi Yesu anawafunsa kuti:+ 42  “Mukuganiza bwanji za Khristu? Kodi ndi mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti: “Ndi mwana wa Davide.”+ 43  Iye anawafunsanso kuti: “Nanga n’chifukwa chiyani mouziridwa ndi mzimu,+ Davide anamutcha ‘Ambuye,’ muja anati, 44  ‘Yehova wauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja kufikira nditaika adani ako kunsi kwa mapazi ako”’?+ 45  Chotero ngati Davide anamutcha kuti ‘Ambuye,’ akukhala bwanji mwana wake?”+ 46  Koma panalibe ngakhale mmodzi amene anatha kumuyankha, ndipo kuchokera tsiku limenelo palibe amene analimbanso mtima kumufunsa mafunso.+

Mawu a M'munsi

Onani Zakumapeto 2.