Mateyu 5:1-48
5 Ataona khamu la anthu, anakwera m’phiri. Atakhala pansi, ophunzira ake anabwera kwa iye.
2 Kenako anayamba kuwaphunzitsa kuti:
3 “Odala ndi anthu amene amazindikira zosowa zawo zauzimu,+ chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.+
4 “Odala ndi anthu amene akumva chisoni, chifukwa adzasangalatsidwa.+
5 “Odala ndi anthu amene ali ofatsa,+ chifukwa adzalandira dziko lapansi.+
6 “Odala ndi anthu amene akumva njala ndi ludzu+ la chilungamo, chifukwa adzakhuta.+
7 “Odala ndi anthu achifundo,+ chifukwa adzachitiridwa chifundo.
8 “Odala ndi anthu oyera mtima,+ chifukwa adzaona Mulungu.+
9 “Odala ndi anthu amene amabweretsa mtendere,+ chifukwa adzatchedwa ‘ana+ a Mulungu.’
10 “Odala ndi anthu amene akuzunzidwa+ chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.
11 “Ndinu odala pamene anthu akukunyozani+ ndi kukuzunzani,+ komanso kukunamizirani zoipa zilizonse chifukwa cha ine.
12 Kondwerani, dumphani ndi chimwemwe,+ chifukwa mphoto+ yanu ndi yaikulu kumwamba, pakuti umu ndi mmenenso anazunzira aneneri+ amene analipo inu musanakhaleko.
13 “Inu ndinu mchere+ wa dziko lapansi. Koma ngati mchere watha mphamvu, kodi mphamvu yake angaibwezeretse motani? Sungagwire ntchito iliyonse koma ungafunike kuutaya kunja+ kumene anthu akaupondaponda.
14 “Inu ndinu kuwala kwa dziko.+ Mzinda ukakhala paphiri subisika.
15 Anthu akayatsa nyale, saivundikira ndi dengu,+ koma amaiika pachoikapo nyale ndipo imaunikira onse m’nyumbamo.
16 Momwemonso, onetsani kuwala+ kwanu pamaso pa anthu, kuti aone ntchito zanu zabwino+ ndi kuti alemekeze+ Atate wanu wakumwamba.
17 “Musaganize kuti ndinabwera kudzawononga Chilamulo+ kapena Zolemba za aneneri. Sindinabwere kudzaziwononga koma kudzazikwaniritsa.+
18 Ndithu ndikukuuzani kuti kumwamba ndi dziko lapansi zingachoke mosavuta,+ kusiyana n’kuti kalemba kochepetsetsa kapena kachigawo kamodzi ka lemba kachoke m’Chilamulo zinthu zonse zisanachitike.+
19 Chotero aliyense wophwanya+ lililonse la malamulo aang’ono awa ndi kuphunzitsa anthu kuphwanya malamulowo, adzakhala ‘wosayenera kulowa’ mu ufumu wakumwamba.+ Koma aliyense wotsatira ndi kuphunzitsa malamulowa,+ ameneyo adzakhala ‘woyenera kulowa’+ mu ufumu wakumwamba.
20 Pakuti ndikukuuzani inu kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha alembi ndi Afarisi,+ ndithudi simudzalowa+ mu ufumu wakumwamba.
21 “Inu munamva kuti anthu akale anauzidwa kuti ‘Usaphe munthu.+ Aliyense amene wapha mnzake+ wapalamula mlandu wa kukhoti.’+
22 Koma ine ndikukuuzani kuti aliyense wopitiriza kupsera mtima+ m’bale wake wapalamula mlandu+ wa kukhoti. Komano aliyense wonenera m’bale wake mawu achipongwe wapalamula mlandu wa ku Khoti Lalikulu. Ndipo aliyense wonena mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe!’ adzapita ku Gehena* wamoto.+
23 “Choncho ngati wabweretsa mphatso yako paguwa lansembe,+ ndipo uli pomwepo wakumbukira kuti m’bale wako ali nawe chifukwa,+
24 siya mphatso yako patsogolo pa guwa lansembe pomwepo. Pita ukayanjane ndi m’bale wako choyamba,+ ndipo ukabwerako, pereka mphatso yako.+
25 “Thetsa nkhani mofulumira ndi munthu wokuimba mlandu pamene ukupita naye kukhoti, kuti mwina wokuimba mlanduyo+ asakakupereke kwa woweruza. Komanso kuti woweruzayo asakakupereke kwa msilikali wa pakhoti kuti akuponye m’ndende.
26 Kunena zoona, sudzatulukamo kufikira utalipira kakhobidi kotsirizira.+
27 “Inu munamva kuti anati, ‘Usachite chigololo.’+
28 Koma ine ndikukuuzani kuti aliyense woyang’anitsitsa mkazi+ mpaka kumulakalaka, wachita naye kale chigololo+ mumtima mwake.+
29 Tsopano ngati diso lako lakumanja limakuchimwitsa,* ulikolowole ndi kulitaya.+ Pakuti n’kwabwino kuti ukhale wopanda chiwalo chimodzi kusiyana n’kuti thupi lako lonse lidzaponyedwe+ m’Gehena.
30 Komanso ngati dzanja lako lamanja limakuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya.+ Pakuti n’kwabwino kuti ukhale wopanda chiwalo chimodzi kusiyana n’kuti thupi lako lonse lidzaponyedwe m’Gehena.
31 “Pajanso anati, ‘Aliyense wothetsa ukwati+ ndi mkazi wake, apatse mkaziyo kalata yothetsera ukwati.’+
32 Koma ine ndikukuuzani kuti aliyense wothetsa ukwati ndi mkazi wake, osati chifukwa cha dama,*+ amamuchititsa chigololo akakwatiwanso,+ ndipo aliyense wokwatira mkazi wosiyidwayo nayenso wachita chigololo.+
33 “Komanso munamva kuti anthu akale anauzidwa kuti, ‘Usamalumbire+ koma osachita, m’malomwake uzikwaniritsa malonjezo ako kwa Yehova.’+
34 Koma ine ndikukuuzani kuti: Usamalumbire+ n’komwe, kutchula kumwamba, chifukwa ndi kumene kuli mpando wachifumu wa Mulungu,+
35 kapena kutchula dziko lapansi chifukwa ndi chopondapo mapazi ake,+ kapena kutchula Yerusalemu chifukwa ndi mzinda+ wa Mfumu yaikulu.
36 Kapena usalumbire kutchula mutu wako, chifukwa sungathe kusandutsa ngakhale tsitsi limodzi kukhala loyera kapena lakuda.
37 Tangotsimikizani kuti mukati Inde akhaledi Inde, ndipo mukati Ayi akhaledi Ayi,+ pakuti mawu owonjezera pamenepa achokera kwa woipayo.+
38 “Inu munamva kuti anati, ‘Diso kulipira diso, ndi dzino kulipira dzino.’+
39 Koma ine ndikukuuzani kuti: Usalimbane ndi munthu woipa, koma wina akakumenya mbama patsaya lakumanja,+ umutembenuzirenso linalo.
40 Ngati munthu akufuna kukutengera kukhoti kuti akulande malaya ako amkati, m’patsenso akunja.+
41 Winawake waudindo akakulamula kuti umunyamulire katundu mtunda wa kilomita imodzi, umunyamulire mtunda wa makilomita awiri.+
42 Munthu akakupempha kanthu m’patse, ndipo munthu wofuna kukongola kanthu kwa iwe popanda chiwongoladzanja usamukanize.+
43 “Inu munamva kuti anati, ‘Uzikonda mnzako+ ndi kudana ndi mdani wako.’+
44 Koma ine ndikukuuzani kuti: Pitirizani kukonda adani anu+ ndi kupempherera amene akukuzunzani,+
45 kuti musonyeze kuti ndinudi ana a Atate wanu wakumwamba.+ Chifukwa iye amawalitsira dzuwa lake pa anthu oipa ndi abwino, ndi kuvumbitsira mvula anthu olungama ndi osalungama omwe.+
46 Pakuti mukamakonda anthu okhawo amene amakukondani, kodi mudzalandira mphoto yotani?+ Kodi okhometsa msonkho sachitanso zimenezo?
47 Ngati mupatsa moni abale anu okha, kodi n’chiyani chachilendo chimene mukuchita? Kodi anthu a mitundu ina nawonso sachita zomwezo?
48 Choncho khalani angwiro, monga mmene Atate wanu wakumwamba alili wangwiro.+