Macitidwe a Atumwi 20:1-38
20 Cipolowe cija citatha, Paulo anaitanitsa ophunzila, ndipo atawalimbikitsa, analailana nao. Kenako anayamba ulendo wake wopita ku Makedoniya.
2 Iye anayenda-yenda m’madela a kumeneko, komanso kulimbikitsa ophunzila ndi mau ambili, kenako anafika ku Girisi.
3 Anakhala kumeneko miyezi itatu. Koma cifukwa cakuti Ayuda anali atamukonzela ciwembu atatsala pang’ono kuyamba ulendo wa panyanja kupita ku Siriya, iye anaganiza zobwelela n’kudzela ku Makedoniya.
4 Pa ulendowo anali ndi Sopaturo mwana wa Puro wa ku Bereya, Arisitako ndi Sekundo a ku Tesalonika, Gayo wa ku Debe, ndi Timoteyo, komanso Tukiko ndi Terofimo ocokela ku cigao ca Asia.
5 Amunawo anatsogola ndipo anali kutiyembekezela ku Torowa.
6 Koma masiku a Mkate Wopanda Zofufumitsa atatha, tinanyamuka ulendo wa panyanja wocoka ku Filipi. Ndipo pambuyo pa masiku asanu tinawapeza ku Torowa kumene tinakhalako masiku 7.
7 Pa tsiku loyamba la mlungu, titasonkhana pamodzi kuti tidye cakudya, Paulo anayamba kuwakambila nkhani cifukwa tsiku lotsatila anali kucoka. Ndipo anakamba kwa nthawi yaitali mpaka pakati pa usiku.
8 M’cipinda capamwamba mmene tinali titasonkhanamo munali nyale zambili.
9 Paulo ali mkati mokamba nkhani, mnyamata wina dzina lake Utiko anakhala pawindo ndipo anagona tulo tofa nato. Ali m’tulo telo, anagwa kucoka pa nsanjika yacitatu ya nyumbayo, ndipo anamupeza atafa.
10 Koma Paulo anatsika n’kufika pamene panali mnyamatayo n’kumukumbatila. Kenako anakamba kuti: “Khalani cete, cifukwa tsopano mnyamatayu ali moyo.”
11 Atatelo Paulo anapitanso m’cipinda capamwamba ndipo anatenga cakudya* n’kuyamba kudya. Kenako anapitiliza kukambilana nao kwa nthawi yaitali mpaka matandakuca. Ndiyeno ananyamuka n’kupita.
12 Conco iwo anatenga mnyamatayo ali wamoyo, ndipo anatonthozedwa kwambili.
13 Tsopano ife tinatsogola kukakwela ngalawa n’kuyamba ulendo wopita ku Aso, koma Paulo anayenda wapansi. Tinamutengela ku Aso malinga ndi mmene anatilangizila.
14 Conco atatipeza ku Aso tinamunyamula m’ngalawa n’kupita ku Mitilene.
15 Tsiku lotsatila tinacoka kumeneko, ndipo tinafika pafupi ndi Kiyo. Koma m’mawa mwake tinaima kwa kanthawi ku Samo, ndipo tsiku lotsatila tinafika ku Mileto.
16 Paulo anaganiza zolambalala Efeso, kuti asataye nthawi m’cigao ca Asia. Iye anali kuthamangila ku Yerusalemu kuti ngati n’kotheka, patsiku la Cikondwelelo ca Pentekosite akakhale kumeneko.
17 Koma ali ku Mileto anatumiza uthenga wakuti akulu a mu mpingo wa ku Efeso abwele.
18 Akuluwo atabwela, iye anawauza kuti: “Inu mukudziwa bwino mmene ndinali kucitila zinthu pakati panu kucokela tsiku loyamba limene ndinafika m’cigao ca Asia.
19 Ndinatumikila Ambuye modzicepetsa kwambili ngati kapolo, ndi misozi, komanso ndi ziyeso zimene ndinakumana nazo cifukwa ca ziwembu za Ayuda.
20 Komabe sindinakubisileni ciliconse cothandiza, ndipo sindinaleke kukuphunzitsani pagulu komanso kunyumba ndi nyumba.
21 Koma ndinacitila umboni mokwanila kwa Ayuda komanso Agiriki kuti alape n’kubwelela kwa Mulungu, komanso kuti ayambe kuika cikhulupililo cao mwa Ambuye wathu Yesu.
22 Ndipo tsopano ndikupita ku Yerusalemu motsogoleledwa* ndi mzimu, ngakhale kuti sindikudziwa zimene zikandicitikile kumeneko.
23 Koma cimene ndikudziwa n’cakuti mu mzinda ndi mzinda, mzimu woyela wakhala ukundicitila umboni mobweleza-bweleza kuti ndikuyembekezela kumangidwa komanso kukumana ndi masautso.
24 Komabe kwa ine moyo wanga sindikuuona monga wofunika, ndingofuna kuti nditsilize kuthamanga mpikisanowu, komanso nditsilize utumiki umene ndinalandila kwa Ambuye Yesu. Kuti ndicitile umboni za uthenga wabwino wa cisomo ca Mulungu.
25 “Tsopano tamvelani! Ndikudziwa kuti nonsenu amene ndinakulalikilani za Ufumu simudzaonanso nkhope yanga.
26 Conco ine ndakuitanani kuti mukhale mboni lelo, kuti ndilibe mlandu wa magazi a anthu onse.
27 Pakuti ndinakuuzani malangizo onse a* Mulungu.
28 Muzidziyang’anila nokha komanso muyang’anile gulu lonse la nkhosa, limene mzimu woyela unakuikani kuti muziliyang’anila, kuti muwete mpingo wa Mulungu umene anaugula ndi magazi a Mwana wake weniweni.
29 Ine ndidziwa kuti ndikapita, mimbulu yopondeleza idzabwela pakati panu, ndipo siidzacitila cifundo gulu la nkhosali.
30 Ndipo pakati panu padzakhala anthu ena amene adzayamba kulankhula zinthu zopotoka n’colinga copatutsa ophunzila kuti aziwatsatila.
31 “Conco khalani maso, ndipo musaiwale kuti kwa zaka zitatu, usana ndi usiku, sindinaleke kucenjeza aliyense wa inu ndikukhetsa misozi.
32 Tsopano Mulungu komanso mau a cisomo cake akutetezeni. Mauwo angakulimbikitseni ndi kukupatsani colowa pakati pa oyela onse.
33 Sindinakhumbile siliva, golide, kapena cobvala ca munthu.
34 Inu mukudziwa kuti manja awa anagwila nchito kuti ndidzipezele zofunikila komanso za anthu amene ndinali nao.
35 Ine ndakuonetsani m’zinthu zonse kuti mwa kugwila nchito molimbika mwa njila imeneyi, muyenela kuthandiza anthu ofooka, komanso muzikumbukila mau a Ambuye Yesu. Iye mwiniyo anati: ‘Kupatsa kumabweletsa cimwemwe cacikulu kuposa kulandila.’”
36 Atakamba izi, iye ndi akulu onsewo anagwada n’kupemphela.
37 Zitatelo, onse analila kwambili, ndipo anakumbatila Paulo ndi kumupsyompsyona mwacikondi.
38 Iwo anamva cisoni kwambili, maka-maka cifukwa ca mau a Paulo akuti iwo sadzaonanso nkhope yake. Kenako anamupelekeza kukakwela ngalawa.

