Cinyanja
Kodi Mungacite Ciani Kuti Mumuyandikile Mulungu?
https://cms-imgp.jw-cdn.org/img/p/1001061100/univ/wpub/1001061100_univ_sqr_xl.jpg
nwt masa. 32-33

FUNSO 18

Kodi Mungacite Ciani Kuti Mumuyandikile Mulungu?

“Inu Wakumva pemphelo, anthu a mitundu yonse adzabwela kwa inu.”

Salimo 65:2

“Uzikhulupilila Yehova ndi mtima wako wonse, ndipo usamadalile luso lako lomvetsa zinthu. Uzimukumbukila mʼnjila zako zonse, ndipo iye adzawongola njila zako.”

Miyambo 3:5, 6

“Iwo adzapeza moyo wosatha akamadziwa za inu Mulungu yekhayo woona, komanso za Yesu Khristu amene inu munamutuma.”

Yohane 17:3

“[Mulungu] kwenikweni sali kutali ndi aliyense wa ife.”

Macitidwe 17:27

“Ine ndikupitiliza kupemphela kuti cikondi canu cizipita cikukulila-kulila, limodzi ndi cidziwitso colondola, komanso luso lanu lozindikila zinthu.”

Afilipi 1:9

“Ngati wina akusowa nzelu, azipempha kwa Mulungu ndipo adzam’patsa, pakuti iye amapeleka kwa onse moolowa manja komanso mosatonza.”

Yakobo 1:5

“Yandikilani Mulungu ndipo iyenso adzakuyandikilani. Yeletsani manja anu ocimwa inu, ndipo yeletsani mitima yanu okaika-kaika inu.”

Yakobo 4:8

“Kukonda Mulungu kumatanthauza kutsatila malamulo ake, ndipo malamulo akewo si olemetsa.”

1 Yohane 5:3