FUNSO 4
Kodi Baibo Imakamba Zolondola pa Nkhani za Sayansi?
“Iye anatambasula thambo lakumpoto pamwamba pa malo opanda kanthu, ndipo dziko lapansi analiika mʼmalele.”
Yobu 26:7
“Mitsinje yonse imakathila mʼnyanja koma nyanjayo sidzaza. Imabwelela kumalo kumene ikucokela kuti ikayambilenso kuyenda.”
Mlaliki 1:7
“Pali winawake amene amakhala pamwamba pa dziko lapansi lomwe ndi lozungulila.”
Yesaya 40:22

