FUNSO 8
Kodi Mulungu Ndiye Amacititsa Kuti Anthu Azibvutika?
“Nʼzosatheka kuti Mulungu woona acite zoipa, kapena kuti Wamphamvuyonse acite zinthu zolakwika.”
Yobu 34:10
“Munthu akakhala pamayeselo asamanene kuti: ‘Mulungu akundiyesa.’ Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi zinthu zoipa ndipo iye sayesa munthu ndi zinthu zoipa.”
“Muzimutulila nkhawa zanu zonse, cifukwa amasamala za inu.”
“Yehova sakucedwa kukwanilitsa lonjezo lake, ngati mmene anthu ena amaonela kuti akucedwa. Koma akuleza nanu mtima cifukwa sakufuna kuti munthu aliyense akaonongedwe, koma akufuna kuti anthu onse alape.”

