Sangandisiye
Pangani Dawunilodi:
1. Ndinangosiidwa,
Ndili ndekhandekha,
Ndilibiletu mzanga,
Ndakhumudwatu kwambiri.
Palibenso munthu,
Wondilimbikitsa,
Ndani anditonthoze?
Ndani andilimbikitse?
(KOLASI)
Ali nane;
Nthawi zonse.
Muli monse,
Sandisiya.
Yehovatu,
Amadziwa.
Amayankha
Mapemphero.
M’mayesero onse,
Sangandisiye.
2. N’ngasiye zambiri
N’khale bwenzi lanu,
Ena ‘ngandilakwire,
Koma inu simusintha
Mwandiyandikira,
Mulidi pafupi.
Ndimakudalirani—
Simungandikhumudwitse.
(KOLASI)
Ali nane;
Nthawi zonse.
Muli monse,
Sandisiya.
Yehovatu,
Amadziwa.
Amayankha
Mapemphero.
M’mayesero onse,
Sangandisiye
Nthawi zonse.
Muli monse,
Sandisiya.
Yehovatu,
Amadziwa.
Amayankha
Mapemphero.
M’mayesero onse,
Sangandisiye.