Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

Sangandisiye

Sangandisiye

Pangani Dawunilodi:

  1. 1. Ndinangosiidwa,

    Ndili ndekhandekha,

    Ndilibiletu mzanga,

    Ndakhumudwatu kwambiri.

    Palibenso munthu,

    Wondilimbikitsa,

    Ndani anditonthoze?

    Ndani andilimbikitse?

    (KOLASI)

    Ali nane;

    Nthawi zonse.

    Muli monse,

    Sandisiya.

    Yehovatu,

    Amadziwa.

    Amayankha

    Mapemphero.

    M’mayesero onse,

    Sangandisiye.

  2. 2. N’ngasiye zambiri

    N’khale bwenzi lanu,

    Ena ‘ngandilakwire,

    Koma inu simusintha

    Mwandiyandikira,

    Mulidi pafupi.

    Ndimakudalirani​—

    Simungandikhumudwitse.

    (KOLASI)

    Ali nane;

    Nthawi zonse.

    Muli monse,

    Sandisiya.

    Yehovatu,

    Amadziwa.

    Amayankha

    Mapemphero.

    M’mayesero onse,

    Sangandisiye

    Nthawi zonse.

    Muli monse,

    Sandisiya.

    Yehovatu,

    Amadziwa.

    Amayankha

    Mapemphero.

    M’mayesero onse,

    Sangandisiye.