GALAMUKANI! April 2014 | Kodi Kudzipha Ndi Njira Yabwino Yothetsera Mavuto?

Kodi munaganizapo zodzipha, kapena pali winawake amene mukumudziwa yemwe anaganizapo zodzipha? Kudziwa zifukwa zokhalira ndi moyo kungathandize kwambiri.

Zochitika Padzikoli

Nkhani zake: mzinda umene maloboti ake awakonza moti azionetsa mtundu wofanana pa nthawi imodzi, vuto la kunenepa lomwe lalowa m’malo mwa vuto la kusowa zakudya m’thupi ndi mbalame ya zaka zoposa 60 yomwe yaswanso mwana wina.

MFUNDO ZOTHANDIZA MABANJA

Kodi Mumatani Wina Akakupatsani Malangizo pa Zomwe Mwalakwitsa?

Kodi zingatheke bwanji kuti malangizo owawa kwambiri akhale othandiza kwambiri?

NKHANI YAPACHIKUTO

Kodi Kudzipha Ndi Njira Yabwino Yothetsera Mavuto?

N’chiyani chingachititse munthu kumaona kuti imfa si mdani?

NKHANI YAPACHIKUTO

Zinthu Zimasintha pa Moyo

Ngakhale zinthu zitakhala kuti sizingasinthe pa moyo wanu, koma pali zimene mungasinthe.

NKHANI YAPACHIKUTO

Pali Zimene Zingakuthandizeni

Pali zifukwa zitatu zokuchititsani kukhalabe ndi moyo.

NKHANI YAPACHIKUTO

Pali Chiyembekezo Choti Zinthu Zidzakhala Bwino M’tsogolo

Chiyembekezo chingakuthandizeni kuiwala mavuto anu.

KUCHEZA NDI ANTHU

Wochita Kafukufuku Wazamankhwala Akufotokoza za Chikhulupiriro Chake

Frédéric Dumoulin ankadana ndi chipembedzo choncho anasiya kukhulupirira zoti kuli Mulungu. Kodi kuphunzira Baibulo komanso kufufuza mmene zamoyo zimagwirira ntchito kunamuthandiza bwanji kuti ayambe kukhulupirira zoti kuli Mlengi?

ANTHU NDI MAYIKO

Dziko la Cambodia

N’chifukwa chiyani anthu oti angokumana koyamba amatchulana kuti achimwene, chemwali, azakhali, amalume kapena agogo?

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Kusankhana Mitundu

Kodi anthu a mitundu yonse ndi ofanana? Kodi kusankhana mitundu kudzatha?

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Mapiko a Gulugufe

Pamwamba pa mapiko a gulugufe ameneyu pamaoneka posalala koma pali tizinthu tomwe mungathe kutiona mutagwiritsa ntchito chipangizo choonera zinthu zing’onozing’ono. Kodi tinthu timeneti n’chiyani?

Zina zimene zili pawebusaiti

Kodi Ndiyenera Kudziwa Zotani pa Nkhani Yotumizirana Mameseji ndi Zinthu Zina Zolaula?

Kodi munthu wina amakukakamizani kuti mumutumizire zolaula? Kodi kutumizirana zolaula kuli ndi mavuto otani? Kodi ndi kukopana basi?

Kodi Ndingatani Anthu Ena Akamandivutitsa?

Anthu ambiri amene akuvutitsidwa amaona kuti palibe chimene angachite. Nkhaniyi ikufotokoza zimene mungachite kuti anthu asiye kukuvutitsani.

Kodi Mnzako Weniweni Ungamudziwe Bwanji?

N’zosavuta kupeza anzanu amene sangakuthandizeni, koma kodi mungapeze bwanji mnzanu weniweni?

Yesefe Anapulumutsa Anthu Ambiri

Nonse monga banja werengani Genesis chaputala 41 mpaka ​50 pogwiritsa ntchito zithunzi za nkhani za m’Baibulo.