NTCHITO YOITANIRA ANTHU KU CHIKUMBUTSO
Yesu Adzathetsa Umphawi
Ali padzikoli, Yesu anasonyeza chikondi chachikulu kwa anthu, makamaka ovutika komanso amene anali ndi nkhawa. (Mateyu 9:36) Iye anafika popereka moyo wake kuti athandize anthuwo. (Mateyu 20:28; Yohane 15:13) Posachedwapa, adzasonyeza umboni winanso wakuti amakonda anthu onse pogwiritsa ntchito mphamvu zake monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu ndipo adzathetsa umphawi padziko lonse lapansi.
Baibulo limafotokoza mwandakatulo zimene Yesu adzachite kuti:
“Ateteze anthu onyozeka pakati pa anthu, Apulumutse ana a anthu osauka.”—Salimo 72:4.
Kodi tingasonyeze bwanji kuti timayamikira zonse zimene Yesu anatichitira komanso zimene adzatichitire posachedwapa? Pa Luka 22:19, Yesu anauza otsatira ake kuti azikumbukira imfa yake. N’chifukwa chake, chaka chilichonse a Mboni za Yehova amakumana pamodzi kuti achite mwambo wokumbukira imfa yake pa tsiku limene anaphedwa. Tikukuitanani kuti mudzakhale nafe Pamwambo Wokumbukira imfa yake Lamlungu pa 24 March 2024.