NSANJA YA OLONDA February 2013 | Kodi Tingaphunzire Chiyani kwa Mose?
Werengani kuti mudziwe makhalidwe atatu mwa makhalidwe abwino amene Mose anali nawo komanso zimene tingaphunzire pa chitsanzo cha Mose.
NKHANI YAPACHIKUTO
Kodi Mose Anali Ndani?
Akhristu, Ayuda, Asilamu komanso anthu ena amalemekeza kwambiri munthu wokhulupirika ameneyu. Kodi inuyo mumadziwa zotani za Mose?
NKHANI YAPACHIKUTO
Mose Anali Munthu Wachikhulupiriro Cholimba
Mose anali ndi chikhulupiriro cholimba chifukwa ankakhulupirira kwambiri zimene Mulungu analonjeza. Kodi ifeyo tingatani kuti tikhale ndi chikhulupiriro ngati chimenechi?
NKHANI YAPACHIKUTO
Mose Anali Munthu Wodzichepetsa
Anthu ambiri amaona kuti munthu wodzichepetsa ndi wofooka. Kodi Mulungu amaona bwanji nkhani ya kudzichepetsa? Kodi Mose anasonyeza bwanji kudzichepetsa?
NKHANI YAPACHIKUTO
Mose Anali Munthu Wachikondi
Mose ankakonda Mulungu komanso aisiraeli anzake. Kodi tingaphunzire chiyani kwa Mose?
YANDIKIRANI MULUNGU
“Iye ndi Mulungu wa Anthu Amoyo”
Mulungu ali ndi mphamvu zothetsa imfa, ndipo walonjeza kudzaukitsa akufa. Kodi Mulungu adzachitadi zimenezi?
BAIBULO LIMASINTHA ANTHU
“Ankafuna Kuti Ndione Ndekha Kuti Zoona Ndi Ziti”
Luis Alifonso ankafuna kudzakhala mmishonale wa chipembedzo cha Mormon. Kodi kuphunzira Baibulo kunamuthandiza bwanji kuti asinthe zolinga zake komanso moyo wake?
CHINSINSI CHA BANJA LOSANGALALA
Zimene Mungachite Ngati Muli ndi Mwana Wolumala
Werengani kuti mumve za mavuto atatu amene mwina mumakumana nawo komanso mmene Baibulo lingakuthandizireni.
Kodi Umene Ena Amati Uthenga Wabwino wa Yudasi N’chiyani?
Kodi analemba ndi Yudasi, wophunzira amene anapereka Yesu? Kodi tiyenera kusintha maganizo pa mmene timaonera Chikhristu chifukwa cha zimene zili mu uthengawu?
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
Popeza Mulungu analenga zonse, kodi iye ndi amene analenga Mdyerekezi? Werengani kuti mudziwe zimene Baibulo limanena.
Zina zimene zili pawebusaiti
Khadi la M’Baibulo Lonena za Esau
Kodi Esau anasonyeza bwanji kuti sankayamikira zinthu zopatulika? Sindikizani khadili kuti mudziwe.
Tsanzirani Msamariya Wachifundo
Werengani fanizo la Msamariya wachifundo ndipo muliganizire mozama kuti muone zimene mungaphunzirepo.