Mika 2:1-13
2 “Tsoka kwa anthu amene amati akagona pabedi, amakonza chiwembu ndiponso kuganiza mmene angachitire zoipa.+ M’mawa kukangocha, iwo amazichitadi+ chifukwa chakuti ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.+
2 Iwo alakalaka minda ya anthu ena ndipo ailanda.+ Alakalakanso nyumba za anthu ena n’kuzitenga kukhala zawo.+ Atenga mwachinyengo cholowa cha munthu ndi cha banja lake.+
3 “Choncho Yehova wanena kuti, ‘Ndikuganiza zobweretsa tsoka pa banja ili.+ Tsoka+ limenelo simudzatha kulipewa,+ moti anthu inu simudzayendanso modzikuza+ chifukwa idzakhala nthawi ya tsoka.+
4 Pa tsikulo munthu adzanena mwambi+ wokhudza anthu inu ndipo ndithu adzakuimbirani nyimbo ya maliro.+ Anthu adzanena kuti: “Ife talandidwa zinthu zathu!+ Cholowa cha anthu amtundu wathu chaperekedwa kwa anthu ena.+ Talandidwa cholowa chathu. Iye wapereka minda yathu kwa anthu osakhulupirika.”
5 Choncho mumpingo wa Yehova simudzapezeka aliyense amene azidzayeza ndi chingwe malo ogawidwa mwa kuchita maere.+
6 Anthu inu musalosere.+ Aneneri amalosera koma sadzalosera zokhudza tsoka limeneli. Ndithu zochititsa manyazi zidzawagwera.+
7 “‘Inu a nyumba ya Yakobo,+ kodi mukunena kuti: “Kodi mzimu wa Yehova sukukhutira, kapena kodi izi ndiye zochita zake?”+ Kodi mawu anga sapindulitsa+ munthu woyenda mowongoka mtima?+
8 “‘Dzulo anthu anga enieni andiukira ngati mdani weniweni.+ Anthu amene akuyenda molimba mtima, ngati anthu obwera kuchokera kunkhondo, muwavule mkanjo wawo wokongola kwambiri umene avala pamwamba pa zovala zawo.
9 Inu mwathamangitsa akazi pakati pa anthu anga, m’nyumba imene mkazi aliyense anali kusangalala kukhalamo. Mwalanda ana awo zinthu zonse zaulemerero+ zimene ndinawadalitsa nazo ndipo simudzazibwezanso mpaka kalekale.*+
10 Nyamukani,+ chokani chifukwa ano si malo opumulirako.+ Dzikoli liwonongedwa chifukwa chakuti ladetsedwa+ ndipo kuwonongedwako kukhala kopweteka.+
11 Munthu wolondola zinthu zopanda pake ndi zachinyengo akanena bodza lakuti:+ “Ndidzakulosererani zokhudza vinyo ndi chakumwa choledzeretsa,” ndiye adzakhale mneneri wa anthu awa.+
12 “‘Ndithu ndidzasonkhanitsa mbadwa zonse za Yakobo.+ Ndidzasonkhanitsa otsala a Isiraeli.+ Ndidzawabweretsa pamalo amodzi ngati gulu la nkhosa m’khola, komanso ngati gulu la ziweto limene lili pamalo amsipu.+ Kumeneko kudzakhala phokoso la anthu.’+
13 “Ndithu wogumula mpanda adzawatsogolera.+ Iwo adzadutsa pogumukapo. Adzatuluka kudutsa pachipata.+ Mfumu yawo idzakhala patsogolo pawo ndipo Yehova adzawatsogolera.”+
Mawu a M'munsi
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.