Mika 1:1-16
1 M’masiku a Yotamu,+ Ahazi+ ndi Hezekiya,+ mafumu a Yuda,+ Yehova analankhula ndi Mika+ wa ku Moreseti kudzera m’masomphenya. M’masomphenyawo anamuuza zokhudza Samariya+ ndi Yerusalemu+ kuti:
2 “Tamverani anthu nonsenu. Mvetsera mwatcheru iwe dziko lapansi ndi anthu onse okhala mwa iwe.+ Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa akhale mboni yokutsutsani pa zimene mukuchita.+ Yehova akutsutseni ali m’kachisi wake woyera.+
3 Tamverani! Yehova akuchoka pamalo ake,+ ndipo atsika ndi kupondaponda m’malo okwezeka a padziko lapansi.+
4 Mapiri asungunuka kumapazi ake+ ndipo zigwa zigawanika. Zonsezi zisungunuka ngati phula losungunuka ndi moto+ ndipo ziyenda ngati madzi othiridwa pamalo otsetsereka.
5 “Izi zichitika chifukwa cha kupanduka kwa Yakobo ndiponso chifukwa cha machimo a nyumba ya Isiraeli.+ Kodi wachititsa kupanduka kwa Yakobo ndani? Kodi si anthu a ku Samariya?+ Wachititsa ndani kuti Yuda akhale ndi malo okwezeka?+ Si anthu a ku Yerusalemu kodi?
6 Samariya ndidzamusandutsa bwinja+ ndi malo oyenera kubzalapo mpesa. Miyala yake ndidzaiponya m’chigwa ndipo maziko ake ndidzawafukula n’kuwasiya pamtunda.+
7 Zifaniziro zake zonse zogoba zidzaphwanyidwa n’kukhala zidutswazidutswa+ ndipo mphatso zonse zimene ankalandira monga malipiro zidzatenthedwa pamoto.+ Mafano ake onse ndidzawawononga. Samariya anapeza zinthu zonsezi ndi ndalama zimene anapeza pochita uhule. Ndipo tsopano zitengedwa kuti zikakhale malipiro a mahule kwinakwake.”+
8 Chifukwa cha zimenezi ndidzalira ndi kufuula.+ Ndidzayenda wopanda nsapato komanso wosavala.+ Ndidzalira ngati mimbulu ndi kumva chisoni ngati nthiwatiwa zazikazi.
9 Zilonda zake n’zosachiritsika+ ndipo zafalikira mpaka kukafika ku Yuda.+ Mliri umenewu wakafika pachipata cha anthu amtundu wanga ku Yerusalemu.+
10 “Anthu inu musanene zimenezi ku Gati ndipo asakuoneni mukulira.+
“Gubudukani pafumbi+ m’nyumba ya Afira.
11 Iwe mkazi wokhala ku Safiri tuluka m’dziko lako uli maliseche mochititsa manyazi.+ Mkazi wokhala ku Zaanana sanachoke m’dziko lake. Beti-ezeli anali malo anu othawirako, koma tsopano kuzingomveka kulira kokhakokha.
12 Mkazi wokhala ku Maroti anali kuyembekezera zinthu zabwino,+ koma zoipa zochokera kwa Yehova zafika pachipata cha Yerusalemu.+
13 Iwe mkazi wokhala ku Lakisi,+ mangirira galeta ku gulu la mahatchi.* Mzinda umenewu ndiwo unayambitsa tchimo la mwana wamkazi wa Ziyoni,+ pakuti kupanduka kwa Isiraeli kwapezeka mwa iwe.+
14 Choncho iwe udzapereka mphatso zotsanzikirana kwa Moreseti-gati.+ Nyumba za Akizibu+ zinali chinthu chokhumudwitsa kwa mafumu a Isiraeli.
15 Iwe mkazi wokhala ku Maresha+ ndidzakubweretsera wolanda zinthu za ena.+ Ulemerero wa Isiraeli udzafika ku Adulamu.+
16 Meta mpala ndi kuchotsa tsitsi lonse chifukwa cha ana ako aamuna amene unali kuwakonda.+ Meta mpala mpaka ufanane ndi wa chiwombankhanga, chifukwa chakuti ana akowo akusiya ndipo apita kudziko lina.”+
Mawu a M'munsi
^ Ena amati “mahosi,” kapena “akavalo.”