GALAMUKANI! July 2013 | Kodi Zionetsero Zimathetsadi Mavuto M’dziko?

Werengani nkhaniyi kuti mudziwe chifukwa chake anthu akumachita zionetsero komanso njira yeniyeni yothetsera mavuto padzikoli.

Zochitika Padzikoli

Muli nkhani monga izi: kusalana polemba ntchito komanso lamulo latsopano lokhudza makampani opanga fodya ku Australia.

MFUNDO ZOTHANDIZA MABANJA

Zimene Mungachite Mwana Akayamba Kuvuta

Kodi mungachite chiyani mwana wanu atayamba kuvuta? Baibulo lili ndi malangizo omwe angakuthandizeni kuthana ndi vuto limeneli.

NKHANI YAPACHIKUTO

Kodi Zionetsero Zimathetsadi Mavuto M’dziko?

Zionetsero zikhozadi kuchititsa kuti zinthu zisinthe. Koma kodi zingathandizedi kuthetsa zinthu zopanda chilungamo, ziphuphu, ndi kuponderezana?

NKHANI YAPACHIKUTO

Ndinaona Kuti Padzikoli Palibe Chilungamo

N’chifukwa chiyani m’nyamata wina wa ku Northern Ireland anasintha maganizo a m’mene mtendere weniweni ungabwerere padzikoli?

Mphaka Wam’tchire Wakuchipululu

Kodi munamvapo za mphaka wam’tchire wakuchipululu? Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zambiri za mphakayu komanso zimene zimachititsa kuti zizikhala zovuta kudziwa kumene wadutsa.

ANTHU NDI MAYIKO

Dziko la Azerbaijan

Anthu a ku Azerbaijan amadziwika kuti ndi okonda kulandira alendo. Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zambiri zokhudza dziko lawo komanso chikhalidwe chawo.

ZIMENE BAIBULO LIMANENA

Ufumu wa Mulungu

Anthu ena amakhulupirira kuti Ufumu wa Mulungu uli m’mitima ya okhulupirira komanso kuti anthu ndi amene adzabweretse Ufumu wa Mulungu. Kodi Baibulo limati chiyani pa nkhaniyi?

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Gologolo wa Ubongo Wodabwitsa Kwambiri

Kodi zimatheka bwanji kuti kanyama kameneka kakhalebe ndi moyo m’madera ozizira kwambiri?

Zina zimene zili pawebusaiti

Kodi Ndingatani Ngati Ndikudwala Matenda Aakulu?—Gawo 2

Werengani zimene achinyamata ena anachita kuti athe kupirira matenda aakulu komanso kuti azikhalabe osangalala.

Nkhani ya Ana a Yakobo

Kodi muyenera kutani ngati m’bale wanu kapena mnzanu wapeza chinthu chimene inuyo mumachifuna kwambiri?