1 Petulo 3:1-22

3  Momwemonso+ inu akazi, muzigonjera+ amuna anu kuti ngati ali osamvera+ mawu akopeke,+ osati ndi mawu, koma ndi khalidwe lanu,+  poona okha ndi maso awo khalidwe lanu loyera+ ndi ulemu wanu waukulu.  Ndipo kudzikongoletsa kwanu kusakhale kwakunja, monga kumanga tsitsi,+ kuvala zodzikongoletsera zagolide,+ kapena kuvala malaya ovala pamwamba.  Koma kukhale kwa munthu wobisika+ wamumtima, atavala zovala zosawonongeka,+ ndizo mzimu wabata ndi wofatsa+ umene uli wamtengo wapatali pamaso pa Mulungu.  Pakuti ndi mmenenso kale akazi oyera amene anali kuyembekeza Mulungu anali kudzikongoletsera. Analinso kugonjera amuna awo,  monga mmene Sara analili womvera kwa Abulahamu, ndipo anali kumutcha kuti “mbuyanga.”+ Tsopano inuyo mwakhala ana ake, ndipo mukhalabe ana ake mukapitiriza kuchita zabwino ndi kusaopa chochititsa mantha chilichonse.+  Inunso amuna,+ pitirizani kukhala ndi akazi anu mowadziwa bwino,+ ndi kuwapatsa ulemu+ monga chiwiya chosalimba, kuti mapemphero anu asatsekerezedwe,+ pakuti mudzalandira nawo limodzi moyo+ umene Mulungu adzakupatseni chifukwa cha kukoma mtima kwake kwakukulu.  Pomaliza, nonsenu mukhale amaganizo amodzi,+ omverana chisoni, okonda abale, achifundo chachikulu,+ ndiponso amaganizo odzichepetsa.+  Osabwezera choipa pa choipa+ kapena chipongwe pa chipongwe,+ koma m’malomwake muzidalitsa,+ chifukwa anakuitanirani njira ya moyo imeneyi, kuti mudzalandire dalitso. 10  Pakuti “amene akufuna kusangalala ndi moyo ndi kuona masiku abwino,+ aletse lilime+ lake kuti lisalankhule zoipa ndi milomo yake kuti isalankhule chinyengo,+ 11  koma aleke zoipa+ ndipo achite zabwino. Ayesetse kupeza mtendere ndi kuusunga.+ 12  Pakuti maso+ a Yehova* ali pa olungama, ndipo makutu ake amamva pembedzero lawo,+ koma nkhope ya Yehova imakwiyira anthu ochita zoipa.”+ 13  Ndithudi, ndani angakuchitireni zoipa mukakhala odzipereka pochita zabwino?+ 14  Koma ngakhale mutavutika chifukwa cha chilungamo, mudzakhalabe odala.+ Musaope zimene iwo amaopa,+ ndipo musade nazo nkhawa.+ 15  Koma vomerezani m’mitima mwanu kuti Khristu ndi Ambuye ndiponso kuti ndi woyera.+ Khalani okonzeka nthawi zonse kuyankha+ aliyense amene wakufunsani za chiyembekezo chimene muli nacho, koma ayankheni ndi mtima wofatsa+ ndiponso mwaulemu kwambiri. 16  Khalani ndi chikumbumtima chabwino,+ kuti ngakhale azikunenerani zoipa ndi kulankhula monyoza za khalidwe lanu labwino monga otsatira Khristu, adzachite manyazi.+ 17  Pakuti ndi bwino kuvutika chifukwa chochita zabwino,+ ngati Mulungu walola, kusiyana ndi kuvutika chifukwa chochita zoipa.+ 18  Pajatu ngakhale Khristu anafera machimo kamodzi kokha basi.+ Munthu wolungamayo anafera anthu osalungama,+ kuti akufikitseni kwa Mulungu.+ Iye anaphedwa m’thupi,+ koma anaukitsidwa monga mzimu.+ 19  Kenako anapita kukalalikira kwa mizimu imene inali m’ndende,+ 20  imene inali yosamvera+ pa nthawi imene Mulungu anali kuleza mtima+ m’masiku a Nowa, pamene chingalawa chinali kupangidwa,+ chimene chinapulumutsa pamadzi anthu owerengeka, miyoyo 8 yokha.+ 21  Chofanana ndi chingalawacho chikupulumutsanso inuyo tsopano.+ Chimenechi ndicho ubatizo, (osati kuchotsa litsiro la m’thupi, koma kupempha chikumbumtima chabwino kwa Mulungu,)+ mwa kuukitsidwa kwa Yesu Khristu.+ 22  Iye ali kudzanja lamanja la Mulungu,+ pakuti anapita kumwamba, ndipo angelo,+ maulamuliro, ndi mphamvu zinakhala pansi pake.+

Mawu a M'munsi

Onani Zakumapeto 2.