1 Petulo 2:1-25
2 Chotero, lekani zoipa zonse,+ zachinyengo zonse, zachiphamaso, kaduka ndi mtundu uliwonse wa miseche.+
2 Koma monga makanda obadwa kumene,+ muzilakalaka mkaka wosasukuluka+ umene uli m’mawu a Mulungu, kuti mwa kumwa mkakawo, mukule ndi kukhala oyenera chipulumutso,+
3 pakuti mwalawa n’kuona kuti Ambuye ndi wokoma mtima.+
4 Pamene mukubwera kwa iye, amene ndiye mwala wamoyo+ umene anthu+ anaukana,+ koma umene Mulungu anausankha, umenenso uli wamtengo wapatali kwa iye,+
5 inunso monga miyala yamoyo mukumangidwa n’kukhala nyumba yauzimu+ kuti mudzakhale ansembe oyera, n’cholinga chakuti mupereke nsembe zauzimu+ zovomerezeka pamaso pa Mulungu kudzera mwa Yesu Khristu.+
6 Pakuti Lemba limati: “Inetu ndikuika mwala m’Ziyoni, mwala wochita kusankhidwa mwapadera, wapakona pa maziko, wamtengo wapatali, ndipo aliyense woukhulupirira sadzakhumudwa.”+
7 Choncho iye ndi wamtengo wapatali kwa inu chifukwa ndinu okhulupirira, koma kwa osakhulupirira, “mwala umene omanga nyumba anaukana,+ umenewu wakhala mwala wapakona wofunika kwambiri,”+
8 komanso “mwala wopunthwitsa ndi thanthwe lokhumudwitsa.”+ Anthu amenewa akupunthwa chifukwa samvera mawu, ndipo anaikidwiratu kale kuti adzatero.+
9 Koma inu ndinu “fuko losankhidwa mwapadera, ansembe achifumu, mtundu woyera,+ anthu odzakhala chuma chapadera,+ kuti mulengeze makhalidwe abwino kwambiri”+ a amene anakuitanani kuchoka mu mdima kulowa m’kuwala kwake kodabwitsa.+
10 Pakuti kale simunali mtundu, koma tsopano ndinu mtundu wa anthu a Mulungu.+ Munali anthu amene sanakuchitireni chifundo, koma tsopano ndinu amene mwachitiridwa chifundo.+
11 Okondedwa, popeza ndinu alendo ndiponso anthu osakhalitsa m’dzikoli,+ ndikukudandaulirani kuti muzipewa zilakolako za thupi+ zimene zili pa nkhondo yolimbana ndi moyo.+
12 Khalani ndi khalidwe labwino pakati pa anthu a m’dzikoli,+ kuti pamene akukunenerani monga anthu ochita zoipa, pa mapeto pake iwo pokhala mboni zimene zikuona ndi maso zochita zanu zabwino,+ adzatamande Mulungu m’tsiku lake loyendera.+
13 Chifukwa cha Ambuye, gonjerani+ dongosolo lililonse lopangidwa ndi anthu:+ kaya mfumu+ chifukwa ili ndi udindo waukulu,
14 kapena nduna chifukwa n’zotumidwa ndi mfumuyo kuti zizipereka chilango kwa ochita zoipa ndi kuyamikira ochita zabwino.+
15 Pakuti chifuniro cha Mulungu n’chakuti, mwa kuchita zabwino muwatseke pakamwa anthu opanda nzeru olankhula zaumbuli.+
16 Khalani mfulu,+ koma ufulu wanu usakhale ngati chophimbira zoipa,+ koma monga akapolo a Mulungu.+
17 Lemekezani anthu, kaya akhale amtundu wotani.+ Kondani gulu lonse la abale,+ opani Mulungu,+ lemekezani mfumu.+
18 Antchito a panyumba akhale ogonjera+ mabwana awo ndi mantha oyenera,+ osati kwa mabwana abwino ndi ololera okha, koma ngakhalenso kwa ovuta kuwakondweretsa.
19 Pakuti zili bwino ngati wina, chifukwa cha chikumbumtima chake kwa Mulungu, akupirira zowawa ndi kuvutika popanda mlandu.+
20 Kodi kupirira kumenyedwa mbama mutachimwa kuli ndi phindu lanji?+ Koma ngati mukupirira povutika chifukwa cha kuchita zabwino,+ zimenezo n’zabwino kwa Mulungu.+
21 Ndipotu anakuitanirani ku moyo umenewu, pakuti ngakhale Khristu anavutika chifukwa cha inu,+ ndipo anakusiyirani chitsanzo kuti mutsatire mapazi ake mosamala kwambiri.+
22 Iye sanachite tchimo,+ ndipo m’kamwa mwake simunapezeke chinyengo.+
23 Pamene anali kunenedwa zachipongwe,+ sanabwezere zachipongwe.+ Pamene anali kuvutika,+ sanawopseze, koma anali kudzipereka kwa iye+ amene amaweruza molungama.
24 Iye ananyamula machimo athu+ m’thupi lake pamtengo,+ kuti tilekane ndi machimo+ n’kukhala amoyo m’chilungamo. Ndipo “munachiritsidwa ndi mabala ake.”+
25 Pakuti munali ngati nkhosa zosochera,+ koma tsopano mwabwerera kwa m’busa+ wanu ndi woyang’anira miyoyo yanu.