Pitani ku nkhani yake

South Korea

 

2018-06-15

SOUTH KOREA

A Mboni za Yehova Anagwira Ntchito Yapadera Yogawira Mabuku Pampikisano wa 2018 wa Olimpiki Komanso wa Anthu Olumala

A Mboni za Yehova ku Korea anagwira ntchito yapadera yogawira mabuku ofotokoza Baibulo kwaulere kwa alendo ochokera m’mayiko ena ku mpikisano wa Olimpiki wa 2018.

2018-04-20

SOUTH KOREA

A Mboni ku South Korea Anapempha Pulezidenti kuti Athetse Kumanga Anthu Okana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira

A Mboni akudikira pamene akuluakulu a boma akuganizira nkhani yokhudza kumanga anthu amene akana usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira.

2018-04-13

SOUTH KOREA

Makhoti a ku South Korea Akufufuza Njira Yabwino Yochitira Zinthu ndi Anthu Okana Usilikali

Oweruza a ku South Korea akufufuza njira yothandizira anthu okana usilikali m’malo mongowamanga. Khoti loona za malamulo lipereka chigamulo pa nkhaniyi.

2016-11-02

SOUTH KOREA

A Mboni za Yehova Omwe Ali M’ndende ku South Korea Aperekanso Madandaulo Ena

Dziko la South Korea likupitiriza kuzunza anyamata omwe ndi a Mboni za Yehova powaika m’ndende chifukwa chogwiritsa ntchito ufulu umene ali nawo wopembedza komanso wochita zinthu mogwirizana ndi zimene amakhulupirira.

2016-08-31

SOUTH KOREA

Kodi Dziko la South Korea Liyamba Kulemekeza Ufulu wa Anthu Wochita Zinthu Mogwirizana ndi Zimene Amakhulupirira?

A Seon-hyeok Kim, omwe ndi a Mboni za Yehova ndipo sagwira ntchito ya usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, poyamba anawapeza kuti ndi wosalakwa pa mlandu woti ankazemba usilikali. N’chifukwa chiyani khoti la apilo linasintha chigamulochi n’kunena kuti a Kim ndi wolakwa?

2016-02-18

SOUTH KOREA

Komiti ina ya United Nations Yapempha Dziko la South Korea Kuti Lipereke kwa Anthu Ufulu Wokana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira

Mayiko ambiri ali ndi chidwi kuti aone ngati boma la South Korea litsatire zimene komiti ya UN yapempha n’kuchita zinthu mogwirizana ndi Pangano la Dziko Lonse la Ufulu wa Anthu ndi wa Zandale.

2016-03-04

SOUTH KOREA

A Mboni a ku Korea Anapereka Madandaulo Awo ku Gulu la United Nations Loona za Anthu Omangidwa Popanda Zifukwa Zomveka

Mayiko ena komanso makhoti a m’dziko la South Korea akufuna kuti dzikolo lisiye kumanga anthu amene amakana usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, m’malo mwake liziwapatsa mwayi wogwira ntchito zina.

2019-03-26

SOUTH KOREA

Khoti Lalikulu ku South Korea Lipereka Chigamulo pa Nkhani ya Anthu Okana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira

Khotili linaimitsa mlanduwu kuti liganize kaye ngati malamulo a asilikali onena kuti anthu okana usilikali ayenera kulandira chilango akugwirizana ndi malamulo a dziko kapena ayi.

2015-12-07

SOUTH KOREA

Dziko la South Korea Lapezeka ndi Mlandu Womanga Anthu Okana Kulowa Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira

Chaka chilichonse, dziko la South Korea limamanga anyamata a Mboni chifukwa chokana kulowa usilikali potsatira zimene amakhulupirira. Komiti Yoona za Ufulu Wachibadwidwe ya Bungwe la United Nations lanenetsa kuti dziko la South Korea lilibe zifukwa zomveka zomangira a Mboniwa. Aka ndi ka nambala 5 kuti komitiyi ikane zifukwazi.

2014-06-27

SOUTH KOREA

Oweruza Milandu Akuvutika Maganizo Poweruza Anthu Okana Kulowa Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira

Oweruza milandu a ku South Korea akuvutika maganizo chifukwa akukakamizika kuweruza mopanda chilungamo anthu amene akukana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, m’malo molemekeza ufulu wawo wachibadwidwe.

2014-04-08

SOUTH KOREA

Kafukufuku Wasonyeza Kuti Anthu a ku South Korea Akufuna Kuti Anthu Okana Kulowa Usilikali Azipatsidwa Ntchito Zina

Anthu ambiri ku Korea akufuna kuti anthu amene amakana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira azipatsidwa ntchito zina.

2013-12-31

SOUTH KOREA

Dziko la South Korea Lasiya Kuphatikiza Anthu Omangidwa pa Nkhani Zokhudza Chikumbumtima Chawo ndi Akaidi Ena Onse

Dziko la South Korea lachepetsako mavuto a anthu ambirimbiri a Mboni za Yehova amene ali kundende chifukwa chokana kulowa usilikali potsatira zimene amakhulupirira.

2013-11-27

SOUTH KOREA

Mayiko ndi Mabungwe Akudzudzula Dziko la South Korea Chifukwa cha Zinthu Zopanda Chilungamo Zimene Likuchita

Kabuku katsopano kofalitsidwa ndi Mboni za Yehova kanafotokoza zokhudza anthu ambirimbiri amene amamangidwa chifukwa chokana kulowa usilikali potengera zimene amakhulupira.