South Korea
A Mboni za Yehova Anagwira Ntchito Yapadera Yogawira Mabuku Pampikisano wa 2018 wa Olimpiki Komanso wa Anthu Olumala
A Mboni za Yehova ku Korea anagwira ntchito yapadera yogawira mabuku ofotokoza Baibulo kwaulere kwa alendo ochokera m’mayiko ena ku mpikisano wa Olimpiki wa 2018.
A Mboni ku South Korea Anapempha Pulezidenti kuti Athetse Kumanga Anthu Okana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira
A Mboni akudikira pamene akuluakulu a boma akuganizira nkhani yokhudza kumanga anthu amene akana usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira.
Makhoti a ku South Korea Akufufuza Njira Yabwino Yochitira Zinthu ndi Anthu Okana Usilikali
Oweruza a ku South Korea akufufuza njira yothandizira anthu okana usilikali m’malo mongowamanga. Khoti loona za malamulo lipereka chigamulo pa nkhaniyi.
A Mboni za Yehova Omwe Ali M’ndende ku South Korea Aperekanso Madandaulo Ena
Dziko la South Korea likupitiriza kuzunza anyamata omwe ndi a Mboni za Yehova powaika m’ndende chifukwa chogwiritsa ntchito ufulu umene ali nawo wopembedza komanso wochita zinthu mogwirizana ndi zimene amakhulupirira.
Kodi Dziko la South Korea Liyamba Kulemekeza Ufulu wa Anthu Wochita Zinthu Mogwirizana ndi Zimene Amakhulupirira?
A Seon-hyeok Kim, omwe ndi a Mboni za Yehova ndipo sagwira ntchito ya usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, poyamba anawapeza kuti ndi wosalakwa pa mlandu woti ankazemba usilikali. N’chifukwa chiyani khoti la apilo linasintha chigamulochi n’kunena kuti a Kim ndi wolakwa?
Komiti ina ya United Nations Yapempha Dziko la South Korea Kuti Lipereke kwa Anthu Ufulu Wokana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira
Mayiko ambiri ali ndi chidwi kuti aone ngati boma la South Korea litsatire zimene komiti ya UN yapempha n’kuchita zinthu mogwirizana ndi Pangano la Dziko Lonse la Ufulu wa Anthu ndi wa Zandale.
A Mboni a ku Korea Anapereka Madandaulo Awo ku Gulu la United Nations Loona za Anthu Omangidwa Popanda Zifukwa Zomveka
Mayiko ena komanso makhoti a m’dziko la South Korea akufuna kuti dzikolo lisiye kumanga anthu amene amakana usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, m’malo mwake liziwapatsa mwayi wogwira ntchito zina.
Khoti Lalikulu ku South Korea Lipereka Chigamulo pa Nkhani ya Anthu Okana Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira
Khotili linaimitsa mlanduwu kuti liganize kaye ngati malamulo a asilikali onena kuti anthu okana usilikali ayenera kulandira chilango akugwirizana ndi malamulo a dziko kapena ayi.
Dziko la South Korea Lapezeka ndi Mlandu Womanga Anthu Okana Kulowa Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira
Chaka chilichonse, dziko la South Korea limamanga anyamata a Mboni chifukwa chokana kulowa usilikali potsatira zimene amakhulupirira. Komiti Yoona za Ufulu Wachibadwidwe ya Bungwe la United Nations lanenetsa kuti dziko la South Korea lilibe zifukwa zomveka zomangira a Mboniwa. Aka ndi ka nambala 5 kuti komitiyi ikane zifukwazi.
Oweruza Milandu Akuvutika Maganizo Poweruza Anthu Okana Kulowa Usilikali Chifukwa cha Zimene Amakhulupirira
Oweruza milandu a ku South Korea akuvutika maganizo chifukwa akukakamizika kuweruza mopanda chilungamo anthu amene akukana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira, m’malo molemekeza ufulu wawo wachibadwidwe.
Kafukufuku Wasonyeza Kuti Anthu a ku South Korea Akufuna Kuti Anthu Okana Kulowa Usilikali Azipatsidwa Ntchito Zina
Anthu ambiri ku Korea akufuna kuti anthu amene amakana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira azipatsidwa ntchito zina.
Dziko la South Korea Lasiya Kuphatikiza Anthu Omangidwa pa Nkhani Zokhudza Chikumbumtima Chawo ndi Akaidi Ena Onse
Dziko la South Korea lachepetsako mavuto a anthu ambirimbiri a Mboni za Yehova amene ali kundende chifukwa chokana kulowa usilikali potsatira zimene amakhulupirira.
Mayiko ndi Mabungwe Akudzudzula Dziko la South Korea Chifukwa cha Zinthu Zopanda Chilungamo Zimene Likuchita
Kabuku katsopano kofalitsidwa ndi Mboni za Yehova kanafotokoza zokhudza anthu ambirimbiri amene amamangidwa chifukwa chokana kulowa usilikali potengera zimene amakhulupira.