Malo a Nkhani

 

2013-08-29

UNITED STATES

A Mboni za Yehova Asaina Pangano Logulitsa Nyumba Zawo ku Brooklyn

A Mboni akugulitsa nyumba zawo zomwe zili ku Brooklyn, zomwe poyamba ankazigwiritsa ntchito posindikiza mabuku awo. Iwo akugulitsanso nyumba yogona yosanja ka 30. Iwo akugulitsa nyumbazi chifukwa akufuna kusamutsira likulu lawo ku Warwick, New York.

2013-08-29

RUSSIA

Khoti la ku Ulaya Lateteza Ufulu wa Mboni za Yehova pa Mlandu Wokhudza Kusungiridwa Chinsinsi

Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya lalamula boma la Russia kuti lipereke chipukuta misozi kwa anthu amene linawaphwanyira ufulu wachibadwidwe wofunika kwambiri wokhudza kusungiridwa chinsinsi.

2013-08-01

UNITED STATES

A Mboni za Yehova Akonzanso Nyumba Yakalekale Yophunzirira Baibulo

A Mboni za Yehova anatsegulira nyumba yakalekale yotchedwa Stanley ku Jersey City, m’chigawo cha New Jersey pambuyo poikonzanso kwa miyezi 6.

2013-11-25

GERMANY

Dziko la Germany Lapereka Mendulo Yaulemu kwa Mayi Wina wa Mboni za Yehova Poyamikira Ntchito Yake Yotamandika

Mathilde Hartl analandira mendulo yaulemu imene boma la Germany limapereka kwa anthu okhawo amene achita zinthu zazikulu. Anapereka menduloyi ndi nduna yaikulu ya chigawo cha Bavaria.

2013-06-30

AUSTRALIA

A Mboni za Yehova Anathandiza Anthu Okhudzidwa ndi Kusefukira kwa Madzi ku Australia

Mphepo yotchedwa Tropical Cyclone Oswald inayambitsa mvula yamphamvu ku Australia. A Mboni za Yehova a m’derali anakhazikitsa komiti yopereka chithandizo kuti ithandize anthu okhudzidwa.

2013-12-31

RUSSIA

Khoti Linagamula kuti, “Sitili M’chaka cha 1937”

Woweruza milandu wa m’bwalo la milandu lalikulu ku Russia anatsutsa chigamulo chimene khoti laling’ono linalamula

2013-12-31

TURKEY

Bungwe la UN Lauza Boma la Turkey Kuti Lizilemekeza Zimene Anthu a M’dzikolo Amakhulupirira

Werengani nkhaniyi kuti mudziwe chigamulo chimene bungwe la UN linapereka chopatsa anthu a ku Turkey ufulu wokana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira.

2014-04-18

ARMENIA

Khoti Lalamula Dziko la Armenia Kuti Lipereke Chipukuta Misozi kwa Anthu 17 a Mboni za Yehova

Pa November 27, 2012, Khoti Loona za Ufulu wa Anthu ku Ulaya linalamula dziko la Armenia kuti lipereke chipukuta misozi cha ndalama zokwana madola 145,226 kwa anthu 17 chifukwa chowaphwanyira ufulu. Anthuwa anakana kulowa usilikali chifukwa cha zimene amakhulupirira.

2014-04-18

UNITED STATES

Kavidiyo: Ku Manhattan Kwayambika Ntchito Yapadera

A Mboni za Yehova ku Manhattan mumzinda wa New York, ayambitsa ntchito yapadera yogawira mabuku awo ofotokoza nkhani za m’Baibulo a m’zinenero zosiyanasiyana. Iwo akumaika mabukuwo pamatebulo omwe akumawaika m’malo osiyanasiyana ku Grand Central Station. Kodi anthu akunena zotani?

2014-04-18

JAPAN

Timavidiyo: Japan: Moyo ukuyambiranso ku Japan patapita chaka chimodzi chivomezi chitachitika

Anthu a Mboni za Yehova akupitiriza kuthandiza anthu amene anapulumuka kutachitika chivomezi ndi madzi osefukira.