Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso

Kabukuka kakonzedwa kuti kakuthandizeni kukhala ndi luso lowerenga pagulu, lolankhula komanso lophunzitsa.

Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira

Timaphunzitsa anthu mfundo zofunika kwambiri kuposa mfundo zina zonse.

PHUNZIRO 1

Mawu Oyamba Abwino

Mawu oyamba abwino amakhala ndi zolinga zitatu.

PHUNZIRO 2

Kulankhula Mokambirana ndi Anthu

Kulankhula mokambirana kumathandiza anthu kuti amasuke komanso atsatire zimene mukunena.

PHUNZIRO 3

Kugwiritsa Ntchito Mafunso

Muzifunsa mafunso abwino kuti anthu achite chidwi komanso kuti mutsindike mfundo zikuluzikulu.

PHUNZIRO 4

Kunena Mawu Oyenera Musanayambe Kuwerenga Lemba

Onani mmene mungathandizire anthu kukonzekera kumva mfundo yapalemba.

PHUNZIRO 5

Kuwerenga Molondola

Kuwerenga molondola kumathandiza kuti anthu adziwe zoona zokhudza Yehova.

PHUNZIRO 6

Kufotokoza Bwino Malemba

Thandizani anthu kuti aone kugwirizana pakati pa lemba limene mwawerenga ndi mfundo imene mukufotokoza.

PHUNZIRO 7

Kulankhula Zoona Komanso Zofika Pamtima

Mukamalankhula zoona komanso zofika pamtima anthu amakhulupirira zimene mukunena.

PHUNZIRO 8

Mafanizo Abwino

Muzigwiritsa ntchito mafanizo osavuta kumva kuti muzifika anthu pamtima komanso kuwathandiza kumvetsa mfundo zofunika.

PHUNZIRO 9

Kugwiritsa Ntchito Bwino Zinthu Zooneka

Muzigwiritsa ntchito zinthu zooneka n’cholinga choti anthu azikumbukira mfundo zanu.

PHUNZIRO 10

Kusinthasintha Mawu

Pena muzilankhula mofulumira, pena mwapang’onopang’ono, pena mokweza, pena motsitsa komanso pena muzilankhula ndi mawu aakulu, pena aang’ono. Muzichita zimenezi n’cholinga choti muzifika anthu pamtima n’kuwathandiza kuti azitsatira zimene akuphunzira.

PHUNZIRO 11

Kulankhula ndi Mtima Wonse

Mukamalankhula ndi mtima wonse mumasonyeza kuti nkhaniyo yakufikani pamtima ndipo zimathandiza kuti anthu azimvetsera mwachidwi.

PHUNZIRO 12

Kulankhula Mwachikondi Komanso Mokoma Mtima

Mukamalankhula mochokera mumtima mumasonyeza anthu kuti mumawakonda.

PHUNZIRO 13

Kusonyeza Kuti Nkhaniyo Ndi Yothandiza

Muzithandiza anthu kumvetsa mmene nkhaniyo imakhudzira moyo wawo komanso mmene angagwiritsire ntchito zimene akuphunzira.

PHUNZIRO 14

Kuthandiza Anthu Kuti Aone Mfundo Zazikulu

Muziwathandiza kuti azitsatira bwinobwino nkhani yanu ndipo aziona kugwirizana pakati pa mfundo yaikulu iliyonse ndi cholinga komanso mutu wa nkhani yanu.

PHUNZIRO 15

Kulankhula Motsimikiza

Muzilankhula motsimikiza. Muzisonyeza kuti mumaona kuti zimene mukunena n’zofunika kwambiri.

PHUNZIRO 16

Kulankhula Molimbikitsa

Muzilankhula zinthu zothandiza osati zokhumudwitsa. Muzifotokoza mfundo zosangalatsa za m’Mawu a Mulungu.

PHUNZIRO 17

Kulankhula Zomveka

Muzithandiza anthu kuti amvetse mfundo zanu. Muzifotokoza mosavuta kumva mfundo zikuluzikulu.

PHUNZIRO 18

Nkhani Yophunzitsadi Anthu

Muzithandiza anthu kuganiza ndiponso kumva kuti aphunzira mfundo zothandiza.

PHUNZIRO 19

Kuwafika Pamtima Anthu

Muzithandiza anthu kukonda Mulungu ndiponso Mawu ake.

PHUNZIRO 20

Mawu Omaliza Abwino

Mawu omaliza abwino amathandiza anthu kukhulupirira zimene aphunzira komanso kuzitsatira.

Zimene Inuyo Mwachita

Muzilemba zimene mwachita poyesetsa kuwerenga ndiponso kuphunzitsa mwaluso.

Mwina Mungakondenso Kudziwa Izi

MAVIDIYO

Mavidiyo a Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso

Pezani luso lowerenga komanso kuphunzitsa pagulu.