MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzidzichepetsa​—Muzipewa Kudzitama

Muzidzichepetsa​—Muzipewa Kudzitama

Munthu akamadzitama amasonyeza kuti ndi wonyada, ndipo zimenezi sizilimbikitsa anthu ena. Choncho Baibulo limati: “Mlendo akutamande, osati pakamwa pako.”​—Miy 27:2.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KHALANI BWENZI LA YEHOVA​—UZIDZICHEPETSA, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi ndi zinthu ziti zimene anthu amadzitama nazo?

  • N’chifukwa chiyani Kalebe amadzitama kwa mnzake?

  • Kodi bambo ake anamuthandiza bwanji kuti azidzichepetsa?

  • Kodi lemba la 1 Petulo 5:5 lingatithandize bwanji kukhala odzichepetsa?