Yoweli 2:1-32
2 “Lizani lipenga m’Ziyoni+ amuna inu ndipo fuulani mfuu yankhondo+ m’phiri langa loyera.+ Anthu onse okhala m’dzikoli anjenjemere,+ pakuti tsiku la Yehova likubwera+ ndipo lili pafupi!
2 Limeneli ndi tsiku lamdima ndi lachisoni,+ tsiku lamitambo ndi lamdima wandiweyani. Tsikuli lili ngati mmene kuwala kwa m’bandakucha kumakhalira pamwamba pa mapiri.+
“Pali mtundu wa anthu ambiri ndiponso amphamvu.+ Palibe mtundu wina umene ungafanane nawo kuyambira nthawi yakale+ ndipo sipadzakhalanso wina wofanana nawo ku mibadwomibadwo.
3 Patsogolo pawo moto wawononga+ ndipo kumbuyo kwawo moto walawilawi ukunyeketsa.+ Patsogolo pawo pali dziko ngati la Edeni+ koma kumbuyo kwawo kuli chipululu chowonongeka ndipo palibe chilichonse chopulumuka.
4 “Mtundu wa anthuwo umaoneka ngati mahatchi,* ndipo amathamanga ngati mahatchi amphamvu.+
5 Amadumphadumpha ndipo amachita mkokomo ngati magaleta oyenda pamwamba pa mapiri+ ndiponso ngati moto walawilawi umene ukutentha mapesi.+ Iwo ali ngati anthu amphamvu amene afola mwa dongosolo lomenyera nkhondo.+
6 Mitundu ya anthu idzamva ululu waukulu+ chifukwa cha mtunduwo, ndipo nkhope zawo zonse zidzakhala zankhawa.+
7 “Amathamanga ngati amuna amphamvu.+ Amakwera khoma ngati amuna ankhondo. Aliyense amayenda m’njira yake ndipo saphonya njira zawo.+
8 Iwo sakankhanakankhana ndipo amayendabe ngati mwamuna wamphamvu amene akuyenda panjira yake. Wina akalasidwa ndi kugwa enawo sabwerera m’mbuyo.
9 “Iwo amathamangira m’mizinda ndipo amathamanga pakhoma la mpanda. Amakwera nyumba ndipo amalowa m’nyumbamo kudzera pawindo ngati mbala.
10 Dziko lanjenjemera pamaso pawo ndipo kumwamba kwagwedezeka. Dzuwa ndi mwezi zada+ ndipo nyenyezi zaleka kuwala.+
11 Yehova adzalankhula+ pamaso pa asilikali ake ankhondo+ pakuti anthu a mumsasa wake ndi ambiri.+ Amene akukwaniritsa mawu ake ali ndi mphamvu. Tsiku la Yehova ndi lalikulu+ ndi lochititsa mantha. Ndani angaime pa tsiku limeneli?”+
12 Yehova wanenanso kuti, “Tsopano bwererani kwa ine ndi mtima wanu wonse.+ Salani kudya,+ lirani momvetsa chisoni ndiponso mokuwa.+
13 Ng’ambani mitima yanu+ osati zovala zanu+ ndipo bwererani kwa Yehova Mulungu wanu pakuti iye ndi wachisomo, wachifundo,+ wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha.+ Ndithu, iye adzakumverani chisoni chifukwa cha tsokalo.+
14 Ndani akudziwa kuti mwina adzasintha maganizo ake ndi kukumverani chisoni+ ndipo kenako adzakusiyirani madalitso,+ nsembe yambewu ndi nsembe yachakumwa kuti mupereke kwa Yehova Mulungu wanu?
15 “Lizani lipenga la nyanga ya nkhosa mu Ziyoni amuna inu.+ Konzekerani nthawi yosala kudya.+ Itanitsani msonkhano wapadera.+
16 Sonkhanitsani anthu onse pamodzi ndipo muyeretse mpingo.+ Sonkhanitsani amuna achikulire. Sonkhanitsani pamodzi ana ndi makanda oyamwa.+ Mkwati atuluke m’chipinda chake ndipo mkwatibwi atuluke kumalo ake ogona.
17 “Ansembe ndi atumiki a Yehova alire m’khonde mwa guwa lansembe+ ndipo anene kuti, ‘Inu Yehova, mverani chisoni anthu anu ndipo musachititse manyazi cholowa chanu+ kuti mitundu ya anthu iwalamulire. Anthu a mitundu ina asanene kuti: “Kodi Mulungu wawo ali kuti?”’+
18 Ndiyeno Yehova adzachitira nsanje dziko lake+ ndipo adzamvera chifundo anthu ake.+
19 Pamenepo Yehova adzayankha ndi kuuza anthu ake kuti, ‘Tsopano ndikukutumizirani mbewu, vinyo watsopano ndi mafuta. Anthu inu mudzakhutadi zinthu zimenezi.+ Ine sindidzakuchititsaninso kukhala chinthu chotonzedwa pakati pa anthu a mitundu ina.+
20 Ndidzakuchotserani mdani wa kumpoto+ kuti akhale kutali ndi inu. Ndidzamuthamangitsira kudziko lopanda madzi ndi labwinja, nkhope yake itayang’ana kunyanja ya kum’mawa*+ ndipo nkhongo yake italoza kunyanja ya kumadzulo.*+ Fungo lake lonunkha lidzamveka ndipo fungo lake loipalo lidzapitirizabe kumveka+ pakuti Mulungu adzachita zinthu zazikulu.’
21 “Usachite mantha iwe dziko. Kondwera ndi kusangalala, pakuti Yehova adzachita zinthu zazikulu.+
22 Inu zilombo zakutchire musachite mantha,+ pakuti malo odyetserako ziweto a m’chipululu adzamera msipu wobiriwira.+ Mitengo nayonso idzabereka zipatso.+ Mtengo wa mkuyu ndi mtengo wa mpesa udzatulutsa zipatso zake zonse.+
23 Inu ana aamuna a Ziyoni kondwerani ndi kusangalala chifukwa cha Yehova Mulungu wanu.+ Iye adzakupatsani mvula yoyambirira pa mlingo woyenera+ ndipo adzakugwetserani mvula yamvumbi, mvula yoyambirira ndi mvula yomaliza, ngati mmene zinalili poyamba.+
24 Malo opunthira mbewu adzadzaza ndi mbewu zopunthidwa ndipo malo ogweramo vinyo watsopano ndi mafuta adzasefukira.+
25 Ndidzakubwezerani mbewu za zaka zonse zimene dzombe ndi ana a dzombe oyenda pansi opanda mapiko, mphemvu ndi mbozi zinadya. Limeneli ndi gulu langa lankhondo lamphamvu limene ndinatumiza pakati panu.+
26 Pamenepo mudzadya ndi kukhuta+ ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu+ amene wakuchitirani zodabwitsa.+ Anthu anga sadzachita manyazi mpaka kalekale.*+
27 Anthu inu mudzadziwa kuti ine ndili pakati pa Isiraeli,+ ndiponso kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu ndipo palibenso Mulungu wina.+ Anthu anga sadzachita manyazi mpaka kalekale.
28 “Zimenezi zikadzachitika ndidzatsanulira mzimu wanga+ pa chamoyo chilichonse,+ ndipo ana anu aamuna ndi ana anu aakazi+ adzanenera. Amuna achikulire adzalota maloto ndipo anyamata adzaona masomphenya.
29 Masiku amenewo ndidzatsanuliranso mzimu wanga pa antchito anu aamuna ndi aakazi.+
30 “Ndidzachita zodabwitsa kuthambo+ ndi padziko lapansi. Ndidzachititsa kuti pakhale magazi, moto ndi utsi wokwera kumwamba.+
31 Dzuwa lidzasanduka mdima,+ ndipo mwezi udzasanduka magazi.+ Zimenezi zidzachitika tsiku lalikulu ndi lochititsa mantha la Yehova lisanafike.+
32 Ndiyeno aliyense woitana pa dzina la Yehova adzapulumuka,+ pakuti m’phiri la Ziyoni ndiponso mu Yerusalemu mudzakhala anthu opulumuka+ monga mmene Yehova ananenera. Amenewa ndi anthu amene Yehova akuwaitana.”+
Mawu a M'munsi
^ Ena amati “mahosi,” kapena “akavalo.”
^ Kutanthauza, “Nyanja Yamchere.”
^ Kutanthauza, “Nyanja Yaikulu.”
^ Onani Matanthauzo a Mawu Ena.