Pitani ku nkhani yake

19 DECEMBER, 2016
RUSSIA

A Mboni za Yehova Achita Apilo pa Chiopsezo Chomwe Anapatsidwa ndi Boma

A Mboni za Yehova Achita Apilo pa Chiopsezo Chomwe Anapatsidwa ndi Boma

Khoti la mumzinda wa Moscow lakonza zodzamvetsera apilo ya Mboni za Yehova ponena za chenjezo lochokera ku boma lomwe likulu lawo lapatsidwa. Pa 16 January, 2017 nthawi ya 11:10 m’mawa, khotili lidzamvetsera apiloyi ndipo mwina lidzapekerekeratu chigamulo chake tsiku lomwelo.

A Mboni akufuna kutsimikizira boma kuti milandu yomwe akuwaimba yoti chipembedzo chawo ndi “kagulu koopsa,” ndi yabodza ndipo ilibe umboni. Milandu yabodzayi yangopekedwa ndi akuluakulu a boma pofuna kusonyeza kuti zinthu zachipembedzo zomwe a Mboniwa amachita mwamtendere, ndi zosemphana ndi malamulo. Pa 12 October, 2016 woweruza milandu m’khoti la Tverskoy mumzinda wa Moscow a M. S. Moskalenko, anakana kumvetsera umboni komanso kuonera vidiyo yomwe inasonyeza zinthu zosemphana ndi malamulo zomwe akuluakulu a boma komanso apolisi anachitira a Mboni.

Loya woona za ufulu wa anthu m’mayiko osiyanasiyana a James Andrik ananena kuti: “Chigamulo chomwe chingaperekedwe chikhala ndi zotsatirapo zazikulu. Ngati khoti la mumzinda wa Moscow lingakane apiloyo, a mu ofesi yozenga milandu adzafuna kuonetsa mphamvu zawo pa chiopsezo chomwe anapereka kulikulu la Mboni. A mu ofesiyi akhoza kutseka likululo komanso kuchitira nkhanza a Mboni onse komanso kuletsa kuti chipembedzo cha Mboni za Yehova chisapezekenso m’dziko lonse la Russia. Koma ngati khotilo lingachite zinthu mogwirizana ndi apiloyo, ndiye kuti chilungamo chioneka.”