Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 156

Ndi Maso a Chikhulupiriro

Ndi Maso a Chikhulupiriro

(Salimo 27:13)

  1. 1. Ndioperenji mkango?

    Ndioperenji anthu?

    Yehovatu alipo

    Ndiopenso chani!

    M’lungu andipulumutsa.

    (KOLASI)

    Ndi masotu a

    chikhulupiriro

    Sindidzaopa

    chilichonsecho.

    Yehovatu alipo

    Sindichita mantha,

    Amakhala nane

    pafupi

    An’thandiza.

  2. 2. Atumiki akale

    Anakhulupirika.

    Chikhulupiriro

    Chinawathandiza.

    M’lungu adzawaukitsa.

    (KOLASI)

    Ndi masotu a

    chikhulupiriro

    Sindidzaopa

    chilichonsecho.

    Yehovatu alipo

    Sindichita mantha,

    Amakhala nane

    pafupi

    An’thandiza.

    (VESI LOKOMETSERA)

    Ndi Yehova,

    zonse ndi

    zotheka.

    Ndili n’chikhulupiriro.

    Chikhulupiriro

    chathandiza kuti

    Ndipirire

    pa mavuto.

  3. 3. M’lungu wandilonjeza

    Tsogolo labwino.

    Ndipirirebe

    Poti posachedwa

    Yehova athetsa mavuto.

    (KOLASI)

    Ndi masotu a

    chikhulupiriro

    Sindidzaopa

    chilichonsecho.

    Yehovatu alipo

    Sindichita mantha,

    Amakhala nane

    pafupi

    An’thandiza.

    An’thandiza.

(Onaninso Aheb. 11:1-40.)