Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 153

Ndithandizeni Ndikhale Wolimba Mtima

Ndithandizeni Ndikhale Wolimba Mtima

(2 Mafumu 6:16)

  1. 1. Ndilitu ndi mantha

    Zinthu zikuvuta.

    M’mavuto m’mandithandiza

    M’makhala pafupi.

    Ndingavutikedi,

    Koma ndikudziwa

    Ndinu wokhulupirika,

    Mudzanditeteza.

    (KOLASI)

    Yehova, mundithandize

    Ndiziona kuti

    Ndizothekatu kupirira

    Ndilimbedi mtima.

    Tili ndi ambiri

    Kuposa ’daniwa.

    Yehova thandizeni

    Muwagonjetsadi.

  2. 2. Ndingachite mantha.

    Pandekha n’zovuta.

    Mumanditeteza ndithu

    Ndidalire inu.

    Mundithandizetu,

    Ndisachite mantha.

    Palibe choti ndiope,

    M’ndende kaya imfa.

    (KOLASI)

    Yehova, mundithandize

    Ndiziona kuti

    Ndizothekatu kupirira.

    Ndilimbedi mtima.

    Tili ndi ambiri

    Kuposa ’daniwa.

    Yehova thandizeni

    Muwagonjetsadi.

    (KOLASI)

    Yehova, mundithandize

    Ndiziona kuti

    Ndizothekatu kupirira.

    Ndilimbedi mtima.

    Tili ndi ambiri

    Kuposa ’daniwa.

    Yehova thandizeni

    Muwagonjetsadi.

    Yehova thandizeni

    Muwagonjetsadi.