Uthenga Wabwino wa Yesu
Mumavidiyowa muphunzira zambiri zokhudza Yesu Khristu mwana wa Mulungu komanso Mpulumutsi.
Zimene Zili M’mavidiyo Akuti; Uthenga Wabwino wa Yesu
Onerani nkhani za m’mabuku a Uthenga Wabwino zomwe zikuoneka ngati zikuchitikadi m’mavidiyo osangalatsa amenewa okhudza Yesu Khristu
GAWO 1
Kuwala Kwenikweni kwa Dziko
Yosefe ndi Mariya akupatsidwa mwayi wamtengo wapatali wolera Yesu, yemwe anali wosiyana ndi ana ena onse.
GAWO 2
“Uyu Ndi Mwana Wanga”
Yohane M’batizi akulengeza za kuonekera kwa Mesiya. Yesu akuyamba utumiki wake.
GAWO 3
“Munthu Ameneyo Ndi Ineyo”
Yesu akuphunzitsa Nikodemo, mayi wa ku Samariya, komanso anthu a ku Nazareti koma anthuwo akulandira uthenga wake mosiyanasiyana.
GAWO 4
“Chifukwa Ndinabwera Kudzachita Zimenezi”
Yesu akuchiritsa odwala, akutulutsa ziwanda, akuphunzitsa anthu komanso akusankha atumwi ake 12.
GAWO 5
“Anadabwa Kwambiri ndi Kaphunzitsidwe Kake”
Pambuyo pochiritsa gulu la anthu, Yesu akuyamba ulaliki wapaphiri womwe ndi wotchuka kwambiri.
GAWO 6
“Kodi Mesiya Amene Tikumuyembekezera uja Ndi Inu?”
Yesu akuukitsa mwana wa mayi wamasiye, akuphunzitsa pogwiritsa ntchito mafanizo osavuta kumva, ndipo akusonyeza poyera zolinga za anthu amene akumumvetsera.

