Sitili Tekha
Daunilodi:
1. Anthu anikana.
Ine navutika.
Nkhawa zaculukitsa.
Moyo wanilemetsadi.
Nilibe anzanga
Anganithandize.
Onitonthoza ndani?
Ndani adzanithandiza?
(KOLASI)
Munalipo, mukalipo
Mudzakhalapo Yehova.
Mumadziŵa, mumaona
Mumamvela Nikapempha.
Olo nivutike, sinili nekha.
2. Olo nivutike cifukwa ca imwe,
Ena anganisiye, koma simunganisiye.
Ndimwe M’lungu wanga.
Mulidi pafupi, nimadalila imwe.
Simunganitailile.
(KOLASI)
Munalipo, mukalipo
Mudzakhalapo Yehova.
Mumadziŵa, mumaona
Mumamvela Nikapempha.
Olo nivutike, sinili nekha.
Munalipo, mukalipo
Mudzakhalapo Yehova.
Mumadziŵa, mumaona
Mumamvela Nikapempha.
Olo nivutike, sinili nekha.