PHUNZILO 11
Kukamba Mwaumoyo
Aroma 12:11
ZOFUNIKILA: Muzikamba mwaumoyo kuti omvela anu akhale ogalamuka komanso olimbikitsidwa.
MOCITILA:
-
Kambani mocokela pa mtima. Pokonzekela nkhani kapena ulaliki wanu, ganizilani za kufunika kwa uthenga wanu. Idziŵeni bwino nkhani yanu cakuti mukaikambe mocokela pa mtima.
-
Ganizilani omvela anu. Ganizilani za mmene mfundo zimene mudzaŵelenga kapena kuphunzitsa zingapindulitsile ena. Onani njila imene mungazifotokozele mowafika pa mtima omvela anu.
-
Ikani umoyo m’nkhani yanu. Kambani mwaumoyo, osati mopola. Pangani magesca acibadwa, komanso nkhope izionetsa mmene mukumvelela.