NYIMBO 14
Tamandani Mfumu Yatsopano Yodzalamulila Dziko
(Salimo 2:12)
-
1. Anthu amitundu yonse asonkhana pamodzi,
Waaitana ni Khristu na odzozedwa ake.
Ufumu wa M’lungu wathu;
Tsopano ulamulila.
Tipempha cifunilo cake,
Cicitike na padziko.
(KOLASI)
Tamandani Yehova; tamandani Yesu—
Mfumu ya Mafumu onse.
Capamodzi timuimbile iye
Ni Mfumu yosatha.
-
2. Titamanda Khristu Mfumu yathu, mosangalala.
Ni Kalonga wa Mtendele adzatipulumutsa.
Taonani madalitso
Ufumu udzabweletsa;
Yesu adzautsa akufa.
Tidzalumpha mokondwela!
(KOLASI)
Tamandani Yehova; tamandani Yesu—
Mfumu ya Mafumu onse.
Capamodzi timuimbile iye
Ni Mfumu yosatha.
(Onaninso Sal. 2:6; 45:1; Yes. 9:6; Yoh. 6:40.)